PHUNZIRO 9
Kugwiritsa Ntchito Bwino Zinthu Zooneka
Genesis 15:5
MFUNDO YAIKULU: Muzigwiritsa ntchito zinthu zooneka kuti anthu amvetse mfundo zikuluzikulu.
MMENE MUNGACHITIRE:
-
Muzisankha zinthu zimene zingathandizedi pophunzitsa. Mungagwiritse ntchito zithunzi, mapu, matchati kapena zinthu zina pofuna kutsindika mfundo zofunika osati timfundo ting’onoting’ono. Mukamaliza, anthu azikumbukira mfundo yaikuluyo osati zinthu zooneka zokhazo.
-
Zinthuzo zizikhala zoti aliyense atha kuziona.