Chitonthozo
Mfundo zotonthoza za m’Baibulo zimene zingatithandize tikakhumudwa
Nkhawa
Onani “Nkhawa”
Kupwetekedwa mtima; kusunga mkwiyo
Anthu ena amasiya kusangalala chifukwa cha mavuto kapena zinthu zopanda chilungamo zimene zikuwachitikira
Onaninso Sl 142:4; Mla 4:1; 7:7
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Malemba otonthoza:
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakutonthozeni:
-
Ru 1:6, 7, 16-18; 2:2, 19, 20; 3:1; 4:14-16—Naomi anayambiranso kusangalala atabwerera kwa anthu a Mulungu wake, atalola kuti ena amuthandize komanso atathandiza anthu ena
-
Yob 42:7-16; Yak 5:11—Yobu anapirira chifukwa cha chikhulupiriro ndipo Yehova anamudalitsa kwambiri
-
Anthu ena amasiya kusangalala chifukwa cha zochita za ena
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
1Sa 1:6, 7, 10, 13-16 —Hana anakhumudwa kwambiri chifukwa cha nkhanza zimene Penina ankamuchitira komanso chifukwa chakuti Mkulu wa Ansembe Eli ankamuganizira kuti waledzera
-
Yob 8:3-6; 16:1-5; 19:2, 3—Anzake atatu a Yobu omwe ankayenera kumutonthoza, ankadziona ngati olungama ndipo anamuweruza molakwika zomwe zinachititsa Yobu kukhumudwa
-
-
Malemba otonthoza:
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakutonthozeni:
-
1Sa 1:9-11, 18—Hana atapemphera kwa Yehova anayamba kumva bwino mumtima
-
Yob 42:7, 8, 10, 17—Yehova anadalitsa Yobu atakhululukira anzake atatu aja
-
Kudziimba kwambiri mlandu
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
2Mf 22:8-13; 23:1-3—Mfumu Yosiya ndi anthu ake anazindikira kulakwa kwawo pamene buku la Chilamulo linkawerengedwa mokweza
-
Eza 9:10-15; 10:1-4—Wansembe Ezara anakhumudwa kwambiri chifukwa choti anthu ena anakwatira akazi achilendo zomwe zinali zosemphana ndi malamulo a Yehova
-
Lu 22:54-62—Mtumwi Petulo atakana Yesu katatu kuti sakumudziwa, anadziimba mlandu kwambiri
-
-
Malemba otonthoza:
-
Onaninso Yes 38:17; Mik 7:18, 19
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakutonthozeni:
-
2Mb 33:9-13, 15, 16—Manase anachita zoipa kwambiri kuposa mafumu ena onse a ku Yuda, komabe analapa ndipo Yehova anamuchitira chifundo
-
Lu 15:11-32—Yesu anafotokoza fanizo la mwana wolowerera pofuna kutiphunzitsa kuti Yehova amakhululuka ndi mtima wonse
-
Kukhumudwa anthu ena akatichitira zinthu zopweteketsa mtima, zokhumudwitsa kapena akatichitira zinthu mosakhulupirika
Onani “Kukhumudwa”
Kukhumudwa chifukwa cha zimene timalakwitsa kapena machimo athu
Onani “Kukhumudwa”
Kudzikayikira kuti ndife osafunika
Onani “Kudzikayikira”
Kudziona kuti sitingakwanitse kupirira vuto linalake lalikulu kapenanso utumiki wovuta
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Malemba otonthoza:
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakutonthozeni:
-
Eks 3:12; 4:11, 12—Yehova anachita zinthu moleza mtima ndi Mose pomutsimikizira kuti amuthandiza kuchita utumiki umene anamupatsa
-
Yer 1:7-10—Yehova anatsimikizira mneneri Yeremiya kuti asachite mantha chifukwa Iye amuthandiza kuchita utumiki wovuta
-
Nsanje; kaduka
Onani “Nsanje”
Kulephera kuchita zambiri chifukwa cha matenda kapena ukalamba
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
2Mf 20:1-3—Mfumu Hezekiya atauzidwa kuti amwalira ndi matenda amene ankadwala, analira kwambiri
-
Afi 2:25-30—Epafurodito anavutika maganizo chifukwa mpingo unali utadziwa kuti iye akudwala choncho anali ndi nkhawa kuti abalewo aona ngati walephera kuchita utumiki wake
-
-
Malemba otonthoza:
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakutonthozeni:
-
2 Sa 17:27-29; 19:31-38—Mfumu inakomera mtima Barizilai, n’kumupempha kuti apitire limodzi ku Yerusalemu, koma modzichepetsa iye anakana kupita podziwa kuti sangakwanitse chifukwa anali wokalamba
-
Sl 41:1-3, 12—Mfumu Davide atadwala kwambiri, anali ndi chikhulupiriro kuti Yehova amuthandiza
-
Mko 12:41-44—Yesu anayamikira mayi wamasiye wosauka chifukwa anapereka zonse zimene anali nazo
-
Kumangoganizira zoipa zimene ena anatichitira
Onani “Kuchitiridwa Zoipa”
Mantha osayenerera; kuopa
Onani “Mantha”
Chizunzo
Onani “Chizunzo”