Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Kulimbikitsana

Kulimbikitsana

N’chifukwa chiyani atumiki a Mulungu amafunika kulimbikitsana?

Yes 35:3, 4; Akl 3:16; 1At 5:11; Ahe 3:13

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • 2Mb 32:2-8​—Pamene Asuri anabwera kudzaopseza Aisiraeli, Mfumu Hezekiya inalimbikitsa anthu ake

    • Da 10:2, 8-11, 18, 19​—Pamene Danieli anali wokalamba komanso wofooka, mngelo anamulimbikitsa

N’chifukwa chiyani Yehova amayembekezera kuti akulu azilimbikitsa anthu ena?

Yes 32:1, 2; 1Pe 5:1-3

Onaninso Mt 11:28-30

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • De 3:28; 31:7, 8​—Mogwirizana ndi malangizo ochokera kwa Yehova, mneneri Mose analimbikitsa Yoswa yemwe anali atatsala pang’ono kulowa m’malo mwake

    • Mac 11:22-26; 14:22​—Mtumwi Paulo ndi Baranaba analimbikitsa Akhristu a ku Antiokeya pa nthawi ya mavuto

N’chifukwa chiyani tikamalimbikitsa anthu ena tiyeneranso kuwayamikira mochokera pansi pa mtima?

Miy 31:28, 29; 1Ak 11:2

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Owe 11:37-40​—Chaka chilichonse, atsikana a mu Isiraeli ankapita kukayamikira mwana wamkazi wa Woweruza Yefita chifukwa anadzimana n’cholinga choti azitumikira panyumba ya Yehova

    • Chv 2:1-4​—Ngakhale kuti Yesu anapereka malangizo kumpingo wa Akhristu a ku Efeso, anawauzanso zinthu zabwino zimene ankachita

Kodi atumiki a Yehova okhulupirika angalimbikitsane m’njira ziti?

Miy 15:23; Aef 4:29; Afi 1:13, 14; Akl 4:6; 1At 5:14

Onaninso 2Ak 7:13, 15, 16

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • 1Sa 23:16-18​—Yonatani anadziwa kuti mnzake Davide akufunika kulimbikitsidwa pa nthawi yomwe anakumana ndi mavuto, choncho anamufunafuna kuti akamulimbikitse

    • Yoh 16:33​—Yesu analimbikitsa ophunzira ake powakumbutsa kuti iye anagonjetsa dziko, choncho nawonso angathe kuligonjetsa ngati akutsatira chitsanzo chake

    • Mac 28:14-16​—Ali pa ulendo wopita kukazengedwa mlandu ku Roma, mtumwi Paulo analimbikitsidwa ataona abale okhulupirika omwe anayenda mtunda wautali kudzakumana naye kuti akamulimbikitse

N’chifukwa chiyani tiyenera kupewa kuchita zinthu mopanda ulemu komanso kumangodandaula zilizonse?

Afi 2:14-16; Yuda 16-19

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Nu 11:10-15​—Mneneri Mose anakhumudwa kwambiri chifukwa cha zinthu zoipa zimene anthu ankachita

    • Nu 13:31, 32; 14:2-6​—Azondi 10 opanda chikhulupiriro atapereka lipoti loipa, anthu anafooka n’kuyamba kuukira

Kodi kupeza nthawi yocheza ndi abale ndi alongo anzathu kumatilimbikitsa bwanji?

Miy 27:17; Aro 1:11, 12; Ahe 10:24, 25; 12:12

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • 2Mb 20:1-19​—Pamene gulu la asilikali linabwera kudzaukira Yuda, Mfumu Yehosafati inaitanitsa anthu onse kuti apemphere limodzi

    • Mac 12:1-5, 12-17​—Mtumwi Yakobo ataphedwa komanso mtumwi Petulo atatsekeredwa m’ndende, anthu amumpingo wa ku Yerusalemu anasonkhana pamodzi kuti apemphere

Kodi kuganizira zokhudza chiyembekezo chathu kumatithandiza bwanji kuti tipirire mayesero amene timakumana nawo?

Mac 5:40, 41; Aro 8:35-39; 1Ak 4:11-13; 2Ak 4:16-18; 1Pe 1:6, 7

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Ge 39:19-23; 40:1-8​—Yosefe anakhalabe wokhulupirika komanso anali wofunitsitsa kuthandiza ena ngakhale kuti anaikidwa m’ndende pa mlandu womunamizira

    • 2Mf 6:15-17​—Mneneri Elisa sanachite mantha gulu lankhondo litawazungulira ndipo anapemphera kuti mtumiki wakenso asachite mantha

Baibulo lingatithandize

Kodi Yehova amatitsimikizira kuti angatithandize bwanji?

Kodi kuganizira kuleza mtima komanso chifundo cha Yehova kungatilimbikitse bwanji?

Kodi Yehova angathandize bwanji anthu amene afooka?

Sl 46:1; Yes 12:2; 40:29-31; Afi 4:13

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • 1Sa 1:10, 11, 17, 18​—Yehova anamvetsera pemphero la Hana ndipo anamuthandiza kuti ayambe kumva bwino pa nthawi imene anakhumudwa kwambiri

    • 1Mf 19:1-19​—Pamene mneneri Eliya anafooka, Yehova anamupatsa chakudya ndi madzi. Kenako, anamulimbikitsa komanso kumutonthoza pomupatsa chiyembekezo chakuti zinthu ziyenda bwino m’tsogolo

Kodi chiyembekezo chimene Baibulo limafotokoza chimatilimbikitsa bwanji?

2Mb 15:7; Sl 27:13, 14; Ahe 6:17-19; 12:2

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Yob 14:1, 2, 7-9, 13-15​—Ngakhale kuti Yobu anadwala matenda aakulu komanso kukumana ndi mavuto osiyanasiyana, anali ndi chikhulupiriro chakuti Yehova akhoza kudzamuukitsa

    • Da 12:13​—Mneneri Danieli, yemwe pa nthawiyo anali ndi zaka pafupifupi 100, analimbikitsidwa ndi mngelo amene anabwera kudzamuuza za madalitso omwe adzalandire m’tsogolo

Kodi kupemphera komanso kuganizira mozama zokhudza Yehova kungatilimbikitse bwanji?

Sl 18:6; 56:4, 11; Ahe 13:6

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • 1Sa 30:1-9​—Davide atakumana ndi mavuto, anapemphera ndipo Yehova anamupatsa mphamvu

    • Lu 22:39-43​—Yesu atakumana ndi mayesero aakulu pa moyo wake, anapemphera kwambiri ndipo Yehova anamuyankha potumiza mngelo kuti adzamulimbikitse

Kodi mauthenga abwino amene timamva angatilimbikitse bwanji? Nanga n’chifukwa chiyani tiyenera kuuza anthu ena?

Miy 15:30; 25:25; Yes 52:7

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Mac 15:2-4​—Mtumwi Paulo ndi Baranaba ankalimbikitsa mipingo pa nthawi imene ankaiyendera

    • 3Yo 1-4​—Mtumwi Yohane ali wokalamba, analimbikitsidwa kwambiri atamva kuti anthu amene anawaphunzitsa choonadi akupitirizabe kukhala okhulupirika