Kusankha Zochita
N’chiyani chingatithandize kuti tizisankha zinthu mwanzeru?
Sl 1:1-3; Miy 19:20; Aro 14:13; 1Ak 10:6-11
Onaninso Eza 7:10
N’chifukwa chiyani sitiyenera kuchita zinthu mopupuluma tikamafuna kusankha zochita pa nkhani zikuluzikulu?
N’chifukwa chiyani tiyenera kupewa kudalira mtima wathu tikamafuna kusankha zochita?
Onaninso Nu 15:39; Miy 14:12; Mla 11:9, 10
-
Nkhani ya m’Baibulo yomwe ingakuthandizeni:
-
2Mb 35:20-24—Mfumu Yosiya yemwe anali munthu wabwino anakana malangizo ochokera kwa Yehova ndipo anapita kukamenya nkhondo ndi Farao Neko
-
N’chifukwa chiyani tiyenera kupemphera kaye tisanasankhe zochita pa nkhani zofunika kwambiri?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Lu 6:12-16—Yesu anapemphera usiku wonse asanasankhe atumwi ake 12
-
2Mf 19:10-20, 35—Mfumu Hezekiya anapemphera kwa Yehova pa nthawi imene ankaopsezedwa ndipo Yehova anamupulumutsa
-
Kodi ndi Ndani amene angatithandize kusankha zinthu mwanzeru kuposa wina aliyense? Nanga angachite bwanji zimenezi?
Sl 119:105; Miy 3:5, 6; 2Ti 3:16, 17
Onaninso Sl 19:7; Miy 6:23; Yes 51:4
-
Nkhani ya m’Baibulo yomwe ingakuthandizeni:
-
Mac 15:13-18—Bungwe lolamulira la ku Yerusalemu linadalira malangizo a m’Malemba posankha zochita pa nkhani ina yaikulu kwambiri
-
Kusankha zochita pa nkhani zokhudza:
Zochitika zonse za moyo wathu
Ntchito
Onani “Ntchito”
Zosangalatsa
Onani “Zosangalatsa”
Ukwati
Onani “Ukwati”
Thandizo la chipatala
Le 19:26; De 12:16, 23; Lu 5:31; Mac 15:28, 29
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Mac 19:18-20—Akhristu a ku Efeso anasiyiratu kuchita zamatsenga komanso zamizimu
-
Zolinga zomwe zingatithandize kukhala pa ubwenzi ndi Yehova
Kugwiritsa ntchito nthawi
Kodi atumiki a Mulungu olimba mwauzimu angatithandize bwanji kuti tizisankha zochita mwanzeru?
Yob 12:12; Miy 11:14; Ahe 5:14
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
1Mf 1:11-31, 51-53—Bati-seba anamvera malangizo a mneneri Natani ndipo mapeto ake anapulumutsa moyo wake ndi wa mwana wake Solomo
-
N’chifukwa chiyani sitiyenera kupempha anthu ena kuti atisankhire zochita?
N’chifukwa chiyani tiyenera kuyesetsa kugwiritsa ntchito malangizo a Mulungu osati kuwakana?
Onaninso Lu 7:30
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Ge 19:12-14, 24, 25—Loti anayesetsa kuchenjeza apongozi ake zokhudza kuwonongedwa kwa mzinda wawo, koma iwo sanamumvere
-
2Mf 17:5-17—Aisiraeli anatengedwa kupita ku ukapolo chifukwa choti ankapitirizabe kukana malangizo a Yehova
-
N’chifukwa chiyani tiyenera kumvera chikumbumtima chathu tikamasankha zochita?
N’chifukwa chiyani ndi bwino kuganizira zotsatirapo za zinthu zomwe tingasankhe?
Mmene zosankha zathu zingakhudzire ena
Mmene zosankha zathu zingakhudzire tsogolo lathu
Onaninso Miy 2:20, 21; 5:3-5
Mmene zosankha zathu zingakhudzire ubwenzi wathu ndi Yehova
N’chifukwa chiyani tiyenera kusamala ndi zimene timasankha?