Makolo
Kodi n’chifukwa chiyani Yehova anayambitsa banja?
Kodi makolo ayenera kuwaona bwanji ana awo?
Onaninso “Ana; Achinyamata”
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Ge 33:4, 5—Yakobo ankaona kuti ana ake ndi madalitso ochokera kwa Yehova
-
Eks 1:15, 16, 22; 2:1-4; 6:20—Amuramu ndi Yokebedi anabereka Mose ndipo iwo analolera kuika moyo wawo pangozi kuti ateteze mwanayo
-
Kodi makolo ayenera kuchitira ana awo zinthu zotani?
N’chifukwa chiyani ndi bwino kuphunzitsa ana kuti azimvera Yehova?
Onaninso 2Ti 3:14, 15
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
1Sa 2:18-21, 26; 3:19 —Makolo a Samueli anapereka mwana wawo kuti azikatumikira kuchihema, komabe iwo ankapita kukamuona komanso kukamupatsa zofunikira; zimenezi zinathandiza kuti akhale munthu wokonda Yehova ndiponso azimutumikira mokhulupirika
-
Lu 2:51, 52—Yesu anapitirizabe kumvera makolo ake ngakhale kuti iwo sanali angwiro
-
Kodi makolo angapeze kuti malangizo ophunzitsira ana awo?
De 6:4-9; Aef 6:4; 2Ti 3:14-17
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Owe 13:2-8—Mngelo atauza Manowa kuti mkazi wake adzakhala ndi mwana, iye anapempha Yehova kuti awapatse nzeru za mmene angalerere mwanayo
-
Sl 78:3-8—Yehova amafuna kuti makolo aziphunzitsa ana awo mfundo za m’Baibulo
-
N’chifukwa chiyani ana amene akulira m’banja lokonda Mulungu amatha kusankha kusatumikira Yehova?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
Kodi makolo ayenera kuyamba liti kuphunzitsa ana awo zimene Mulungu amafuna kuti azichita?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
De 29:10-12, 29; 31:12; Eza 10:1—Aisiraeli akasonkhana pamodzi kuti aphunzire zokhudza Yehova, ankakhala limodzi ndi ana awo
-
Lu 2:41-52—Chaka chilichonse, Yosefe ndi Mariya ankatenga ana awo kuphatikizapo Yesu popita kuchikondwerero cha Pasika kukachisi wa ku Yerusalemu
-
Kodi makolo ayenera kutsatira zitsanzo ziti pamene akufuna kuteteza ana awo kwa anthu amene angawachitire nkhanza?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Eks 19:4; De 32:11, 12—Yehova anadziyerekezera ndi chiwombankhanga chimene chimanyamula, kuteteza komanso kusamalira ana ake
-
Yes 49:15—Yehova analonjeza kuti adzasamalira komanso kuteteza atumiki ake kuposa mmene mayi woyamwitsa amasamalirira mwana wake wakhanda
-
Mt 2:1-16—Satana ankafuna kupha Yesu ali wakhanda potsogolera anthu okhulupirira nyenyezi kwa Mfumu Herode, koma Yehova anateteza Mwana wake pouza Yosefe kuti athawire ku Iguputo
-
Mt 23:37—Yesu anasonyeza kuti ndi wofunitsitsa kuthandiza anthu ake mofanana ndi mmene nkhuku yathadzi imatetezera ana ake powabisa m’mapiko
-
N’chifukwa chiyani makolo ayenera kuphunzitsa ana awo nkhani zokhudza kugonana?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Le 15:2, 3, 16, 18, 19; De 31:10-13—Chilamulo cha Mose chinkanena mosapita m’mbali nkhani zokhudza kugonana ndipo Yehova analamula kuti ana azimvetsera nawo Chilamulochi chikamawerengedwa mokweza
-
Sl 139:13-16—Wamasalimo Davide anatamanda Yehova chifukwa cha mmene thupi la munthu linalengedwera modabwitsa komanso m’njira yoti anthu azitha kubereka ana
-
Miy 2:10-15—Kudziwa zinthu komanso nzeru zochokera kwa Yehova zingatiteteze kwa anthu oipa komanso achinyengo
-
N’chifukwa chiyani makolo ayenera kulangiza kapena kuphunzitsa ana awo mwachikondi?
Miy 13:24; 29:17; Yer 30:11; Aef 6:4
Onaninso Sl 25:8; 145:9; Akl 3:21
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Sl 32:1-5—Yehova anapereka chilango kwa Mfumu Davide chifukwa cha tchimo lomwe anachita komabe analimbikitsidwa atadziwa kuti Yehova amakhululukira anthu omwe alapa kuchokera pansi pa mtima
-
Yon 4:1-11—Mneneri Yona analankhula kwa Yehova mopsa mtima komanso mopanda ulemu; komabe Yehova anamulezera mtima pofuna kumuphunzitsa kuti Iye ndi wachifundo
-
N’chifukwa chiyani tinganene kuti makolo amasonyeza chikondi akamapereka chilango kwa ana awo?
Onaninso Miy 15:32; Chv 3:19