Oyang’anira
Kodi akulu mumpingo afunika kumachita zotani kuti akhale oyenerera komanso kuti apitirize udindo wawo?
Kodi akulu mumpingo ayenera kuchitanso zinthu ziti posonyeza chitsanzo chabwino?
Mt 28:19, 20; Aga 5:22, 23; 6:1; Aef 5:28; 6:4; 1Ti 4:15; 2Ti 1:14; Tit 2:12, 14; Ahe 10:24, 25; 1Pe 3:13
Kodi atumiki othandiza mumpingo ayenera kukwaniritsa zinthu ziti?
Kodi mzimu wa Yehova umathandiza bwanji abale posankha oyang’anira?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Mac 13:2-5; 14:23—Paulo ndi Baranaba ankasankha akulu m’mipingo yosiyanasiyana; n’chimodzimodzinso oyang’anira masiku ano. Iwo amapempha mzimu woyera kuti uwathandize kumvetsa bwino Malemba kuti athe kusankha bwino anthu omwe ali oyenerera kukhala pa udindo
-
Tit 1:1, 5—Tito anapatsidwa ntchito yoyendera mipingo yosiyanasiyana kuti asankhe akulu
-
Kodi mpingo ndi wa ndani? Nanga unagulidwa pa mtengo wotani?
N’chifukwa chiyani Baibulo limatchula akulu kuti atumiki, kapena kuti akapolo otumikira ena?
N’chifukwa chiyani oyang’anira afunika kukhala odzichepetsa?
Afi 1:1; 2:5-8; 1At 2:6-8; 1Pe 5:1-3, 5, 6
-
Nkhani ya m’Baibulo yomwe ingakuthandizeni:
-
Mac 20:17, 31-38—Mtumwi Paulo anakumbutsa akulu a ku Efeso zimene anawachitira kwa zaka zambiri ndipo iwo anasonyeza kuyamikira chikondi chake
-
Kodi oyang’anira ayenera kuona bwanji malangizo ochokera kwa “kapolo wokhulupirika komanso wanzeru”?
Kodi ndi njira yabwino kwambiri iti yomwe akulu angaphunzitsire ena?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Ne 5:14-16—Chifukwa choopa Yehova, Bwanamkubwa Nehemiya anapewa kugwiritsa ntchito udindo wake molakwika pakati anthu a Mulungu ngakhalenso kutenga zinthu zimene zinayenera kuperekedwa kwa iye
-
Yoh 13:12-15—Zimene Yesu anachita kwa otsatira ake zinawaphunzitsa kukhala odzichepetsa
-
Kodi abusa a Chikhristu angasonyeze bwanji kuti amadera nkhawa wina aliyense mumpingo?
Kodi akulu angathandize bwanji Mkhristu yemwe akudwala mwauzimu?
Kodi akulu ali ndi udindo wotani pa nkhani yophunzitsa?
1Ti 1:3-7; 2Ti 2:16-18; Tit 1:9
Onaninso 2Ak 11:2-4
N’chifukwa chiyani akulu ayenera kuchita khama poonetsetsa kuti mpingo ndi woyera?
1Ak 5:1-5, 12, 13; Yak 3:17; Yuda 3, 4; Chv 2:18, 20
Onaninso 1Ti 5:1, 2, 22
Kodi ayenera kuchita khama pophunzitsa ndani?
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Mt 10:5-20—Yesu anaphunzitsa otsatira ake 12 kenako anawatumiza kuti akagwire ntchito yolalikira
-
Lu 10:1-11—Yesu anapereka kaye malangizo kwa ophunzira ake 70 asanawatumize kukagwira ntchito yolalikira
-
N’chiyani chingathandize akulu kukwaniritsa ntchito zawo zosiyanasiyana?
Onaninso Miy 3:5, 6
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
1Mf 3:9-12—Solomo atakhala mfumu, anapempha kwa Yehova kuti amupatse nzeru komanso mtima womvetsa zinthu kuti amuthandize kuweruza anthu a Yehova
-
2Mb 19:4-7—Mfumu Yehosafati anasankha oweruza m’mizinda ya Yuda ndipo anawakumbutsa kuti Yehova adzakhala nawo pa nthawi imene akugwira ntchito yawo
-
Kodi Akhristu ayenera kuwaona bwanji akulu okhulupirika?
1At 5:12, 13; 1Ti 5:17; Ahe 13:7, 17
-
Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:
-
Mac 20:37—Akhristu a ku Efeso sankazengereza kusonyeza chikondi chawo kwa mtumwi Paulo
-
Mac 28:14-16—Pamene mtumwi Paulo ankayenda maulendo opita ku Roma, abale amumzindawo anayenda ulendo wa makilomita 65 kuti adzakumane naye ku Msika wa Apiyo ndipo anamulimbikitsa kwambiri
-