Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Yehova Analenga Angelo Ambirimbiri

Yehova Analenga Angelo Ambirimbiri

Baibulo limanena kuti Yehova ndi mzimu. Iye analenganso angelo ambirimbiri omwe ali ndi matupi auzimu.​—Yohane 4:24; 2 Akorinto 3:17, 18.

Poyambirira, Yehova analipo yekha. Kenako anayamba kulenga angelo omwe ndi amphamvu komanso anzeru kuposa anthufe. Angelowa alipo ambirimbiri ndipo Danieli anaona m’masomphenya angelo okwana 100 miliyoni.​—Danieli 7:10; Aheberi 1:7.

Angelowa analengedwa dziko lapansili lisanalengedwe. (Yobu 38:4-7) Iwowa si anthu amene anamwalira padzikoli n’kupita kumwamba.

Yehova analenga angelo ambirimbiri