Mupeze Mayankho a Mafunso Awa
1. Kodi ndi zinthu zitatu ziti zimene Yehova amatichitira kuti tizisangalala? (Sl 32:1-10)
2. Kodi tingatani kuti tizisangalala panopa? (Sl 5:11, 12; 91:14)
3. Kodi tingatani kuti tizisangalala pa utumiki wathu ngakhale kuti tikukumana ndi mavuto? (Mac 13:50-52; Aro 5:3-5)
4. Kodi tingatani kuti tipewe ‘kulemedwa’ n’kumakhala osasangalala? (Lu 21:34)
5. Kodi Yehova amatithandiza bwanji kuti tizikhala osangalala? (Sl 92:4, 5)
6. N’chiyani chingatithandize kuti tiziika Yehova patsogolo pathu nthawi zonse? (Aro 1:20; De 6:6-9; Afi 4:6; Sl 16:3)