Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

MUTU 5

“Chuma Chonse Chokhudzana ndi Nzeru”

“Chuma Chonse Chokhudzana ndi Nzeru”

1-3. Kodi Yesu analalikira pamalo ati mu 31 C.E. ndipo zinthu zinali bwanji pa nthawiyo, nanga n’chifukwa chiyani omvera ake anadabwa kwambiri?

 CHINALI chaka cha 31 C.E. ndipo Yesu Khristu anali paphiri linalake lomwe lili pafupi ndi mzinda wa Kaperenao. Mzindawu unali kumpoto chakumadzulo kwa nyanja ya Galileya ndipo unali wotchuka kwambiri. Yesu anali yekhayekha kuphiri limeneli ndipo anapemphera usiku wonse. Kunja kutacha, anaitana ophunzira ake n’kusankhapo anthu 12 omwe anawatchula kuti atumwi. Pa nthawiyi, anthu ambiri, ena mwa iwo ochokera m’madera a kutali, anatsatira Yesu kumalo amene iye anali ndipo anasonkhana pamalo afulati paphiripo. Iwo ankayembekezera mwachidwi kuti amvetsere Yesu akamaphunzitsa komanso kuti awachiritse matenda awo osiyanasiyana. Ndipo Yesu anachitadi zimene anthuwo ankayembekezera.​—Luka 6:12-19.

2 Yesu anapita pamene panali anthuwo n’kuchiritsa aliyense amene ankadwala. Kenako iye anakhala pansi n’kuyamba kuwaphunzitsa. a Anthuwo ayenera kuti anadabwa ndi mmene iye ankaphunzitsira chifukwa anali asanamvepo munthu wina aliyense akuphunzitsa ngati mmene Yesu anachitira. Pofuna kusonyeza kuti zimene ankaphunzitsazo n’zofunika kwambiri, Yesu sanaikemo miyambo ya Ayuda kapena zinthu zimene arabi otchuka a Chiyuda ankaphunzitsa. Koma mobwerezabwereza, iye ankagwira mawu Malemba a Chiheberi ouziridwa. Uthenga wake unali wosapita m’mbali komanso unali womveka bwino ndipo iye ankagwiritsa ntchito mawu osavuta kumva. Atamaliza kuphunzitsa, anthuwo anadabwa kwambiri. Mpake kuti iwo anadabwa chifukwa anali atamvetsera ulaliki wa munthu wanzeru kwambiri kuposa aliyense padziko lapansi.​—Mateyu 7:28, 29.

“Gulu la anthulo . . . linadabwa ndi kaphunzitsidwe kake”

3 Ulaliki umenewu limodzi ndi zinthu zina zambiri zimene Yesu ananena ndi kuchita, zinalembedwa m’Baibulo, lomwe ndi Mawu a Mulungu. Tingachite bwino kufufuza mozama Mawu a Mulungu kuti tidziwe mfundo zina zokhudza Yesu, chifukwa “chuma chonse chokhudzana ndi nzeru” chili mwa iye. (Akolose 2:3) Yesu anali ndi nzeru ndipo zochita zake zinkasonyeza kuti ankadziwa zinthu zambiri komanso anali wozindikira. Kodi nzeru zimenezo anazitenga kuti? Kodi iye anasonyeza bwanji kuti anali ndi nzeru, nanga ifeyo tingamutsanzire bwanji?

“Kodi Munthu Ameneyu Anazitenga Kuti . . . Nzeru Zimenezi?”

4. Kodi anthu amene ankamvetsera Yesu ku Nazareti anafunsa funso lotani, nanga n’chifukwa chiyani?

4 Pa nthawi ina Yesu ali pa ulendo wolalikira m’madera osiyanasiyana, anafika ku Nazareti, mzinda umene iye anakulira, n’kuyamba kuphunzitsa m’sunagoge. Ambiri mwa anthu amene ankamumvetsera anadabwa ndipo anafunsa kuti: “Kodi munthu ameneyu anazitenga kuti . . . nzeru zimenezi?” Iwo ankawadziwa bwino makolo ake komanso abale ake ndipo ankadziwanso kuti anachokera m’banja losauka. (Mateyu 13:54-56; Maliko 6:1-3) Anthuwo ayenera kuti ankadziwanso kuti kalipentala wodziwa kuphunzitsa Mawu a Mulungu ameneyu sanaphunzire m’sukulu zotchuka za arabi. (Yohane 7:15) Choncho m’pomveka kuti iwo anafunsa funso limeneli.

5. Kodi Yesu anaulula kuti nzeru zake zinachokera kwa ndani?

5 Ngakhale kuti Yesu anali wangwiro, nzeru zimene anasonyeza pophunzitsa sizinkachokera m’mutu mwake. Pa nthawi ina Yesu akuphunzitsa m’kachisi, anaulula kuti nzeru zake n’zochokera kwa winawake wanzeru kwambiri kuposa iyeyo. Iye anati: “Zimene ine ndimaphunzitsa si zanga, koma ndi za amene anandituma.” (Yohane 7:16) Choncho, nzeru za Yesu zinachokera kwa Atate wake amene anamutuma. (Yohane 12:49) Komabe, kodi Yesu analandira bwanji nzeru zochokera kwa Yehova?

6, 7. Kodi Yesu analandira nzeru zochokera kwa Atate ake m’njira ziti?

6 Mzimu woyera wa Yehova unakhazikika mumtima ndi m’maganizo a Yesu. Polosera za Mesiya wolonjezedwa, amene ndi Yesu, Yesaya ananena kuti: “Mzimu wa Yehova udzakhazikika pa iye, mzimu wanzeru ndi womvetsa zinthu, mzimu wopereka malangizo abwino ndi wamphamvu, mzimu wodziwa zinthu ndi woopa Yehova.” (Yesaya 11:2) Choncho, n’zosadabwitsa kuti mawu komanso zochita za Yesu zinasonyeza kuti anali ndi nzeru zakuya chifukwa mzimu woyera wa Yehova unali pa iye ndipo unkatsogolera maganizo ake ndiponso zinthu zimene ankasankha kuchita.

7 Yesu analandira nzeru kuchokera kwa Atate ake m’njira inanso yapadera kwambiri. Mogwirizana ndi zimene tinaona m’mutu wachiwiri, iye anakhala zaka zosawerengeka ndi Atate ake kumwamba asanabwere padziko lapansi. Pa nthawiyi, Yesu anali ndi mwayi wodziwa maganizo a Atate ake pa nkhani zosiyanasiyana. Sitingathe n’komwe kudziwa kuya kwa nzeru zimene Mwanayu anatengera kwa Atate ake. Iye anatengera nzeruzi kwa Mulungu pamene ankagwira ntchito yolenga zinthu zonse, zamoyo komanso zopanda moyo, monga ‘mmisiri wake waluso.’ Choncho, n’zomveka kuti Baibulo limafotokoza kuti Mwanayu asanabwere padziko lapansi anali ngati nzeru. (Miyambo 8:22-31; Akolose 1:15, 16) Pa utumiki wake wonse, Yesu ankagwiritsa ntchito nzeru zimene anatengera kwa Atate ake pa nthawi imene anali kumwamba. b (Yohane 8:26, 28, 38) Choncho, sitiyenera kudabwa kuti pa mawu aliwonse ndiponso pa chilichonse chimene ankachita, Yesu anasonyeza nzeru zakuya komanso kumvetsa zinthu.

8. Monga otsatira a Yesu, kodi tingatani kuti tipeze nzeru?

8 Monga otsatira a Yesu, nafenso tiyenera kudalira Yehova kuti azitipatsa nzeru. (Miyambo 2:6) Komabe, Yehova sangatipatse nzeru mozizwitsa. M’malomwake iye amayankha mapemphero athu ochokera pansi pa mtima opempha nzeru zimene zingatithandize kuti tizilimbana ndi mavuto pa moyo wathu. (Yakobo 1:5) Pamafunika khama kuti tipeze nzeru zimenezi, choncho tiyenera kupitiriza kuzifunafuna “ngati chuma chobisika.” (Miyambo 2:1-6) Ndithudi, tikuyenera kupitiriza kuphunzira mwakhama Mawu a Mulungu kuti tipeze nzeru zimenezi ndipo tizichita zinthu mogwirizana ndi zimene taphunzirazo. Njira imodzi yabwino kwambiri imene ingatithandize kupeza nzeru ndi kuganizira chitsanzo cha Yesu, amene ndi Mwana wa Yehova. Tiyeni tione mbali zingapo zimene Yesu anasonyezera nzeru ndipo tiphunzira zimene tingachite kuti timutsanzire.

Mawu a Nzeru

Baibulo limasonyeza nzeru zimene Mulungu ali nazo

9. N’chiyani chinachititsa kuti zinthu zimene Yesu ankaphunzitsa zikhale za nzeru?

9 Anthu ambirimbiri ankapita kwa Yesu kukamumvetsera akamaphunzitsa. (Maliko 6:31-34; Luka 5:1-3) Ndipo zimenezi n’zosadabwitsa chifukwa Yesu ankati akayamba kulankhula, mawu ake ankakhala a nzeru zosaneneka. Zinthu zimene ankaphunzitsa zinasonyeza kuti ankadziwa bwino kwambiri Mawu a Mulungu komanso ankawadziwa bwino anthu. Zimene ankaphunzitsa zikugwirabe ntchito mpaka lero ndipo n’zothandiza kwa munthu aliyense. Taonani zina mwa zitsanzo zosonyeza nzeru za Yesu, “Mlangizi Wodabwitsa,” amene Yesaya anamulosera.​—Yesaya 9:6.

10. Kodi Yesu anatilimbikitsa kuti tikhale ndi makhalidwe abwino ati, nanga n’chifukwa chiyani?

10 Ulaliki wa paphiri, umene tautchula kumayambiriro kwa nkhani ino, ndi ulaliki wautali kwambiri pa maulaliki onse a Yesu amene analembedwa m’Baibulo. Mu ulalikiwu mulibe mawu ofotokozera kapena mawu a anthu ena. Sikuti Yesu anangopereka malangizo okhudza kulankhula mwaulemu komanso kukhala ndi khalidwe labwino, koma ananenanso zimene zingatithandize kuchita zimenezi. Chifukwa choti Yesu ankadziwa kuti anthufe timalankhula komanso kuchita zinthu zimene zili mumtima ndi m’maganizo mwathu, iye anatilimbikitsa kuti tiziyesetsa kukhala ndi makhalidwe abwino, amene amayambira mumtima ndi m’maganizo. Ena mwa makhalidwe amenewa ndi kufatsa, chilungamo, chifundo, mtendere ndiponso kukonda anthu ena. (Mateyu 5:5-9, 43-48) Tikamayesetsa kukhala ndi makhalidwe amenewa mumtima mwathu, khalidwe lathu ndiponso zolankhula zathu zimasangalatsa Yehova komanso timakhala pa ubwenzi wabwino ndi anthu ena.​—Mateyu 5:16.

11. Popereka malangizo amene amatithandiza kupewa makhalidwe oipa, kodi Yesu anasonyeza bwanji kufunika kolimbana ndi chimene chimayambitsa vuto?

11 Pamene ankapereka malangizo othandiza kuti tizipewa makhalidwe oipa, Yesu anatchula zimene zimayambitsa makhalidwe oipawo. Mwachitsanzo, iye sanangotiuza kuti tizipewa kuchita zachiwawa. M’malomwake, anatichenjeza kuti tizipewa kusunga mkwiyo mumtima mwathu. (Mateyu 5:21, 22; 1 Yohane 3:15) Kuwonjezera pa kuletsa kuchita chigololo, iye anatichenjeza kuti tizipewa maganizo oipa amene amayambira mumtima omwe amachititsa kuti munthu achite tchimoli. Komanso anatichenjeza kuti tisamalole kuti maso athu azitichititsa kukhala ndi chilakolako choipa chogonana. (Mateyu 5:27-30) Yesu anatiphunzitsa kufunika kolimbana ndi chimene chimayambitsa vuto, osati kungolimbana ndi vuto lokhalo. Iye anapereka malangizo amene amatithandiza kuthana ndi makhalidwe ndiponso mtima umene ungatilimbikitse kuchita tchimo.​—Salimo 7:14.

12. Kodi otsatira a Yesu amaona bwanji malangizo amene iye anapereka, ndipo n’chifukwa chiyani?

12 Mawu a Yesu anasonyeza nzeru zakuya kwambiri. Choncho n’zosadabwitsa kuti “gulu la anthulo . . . linadabwa ndi kaphunzitsidwe kake.” (Mateyu 7:28) Monga otsatira ake, timagwiritsa ntchito malangizo akewo kuti azitithandiza pa moyo wathu. Timayesetsa kukhala ndi makhalidwe abwino amene iye analimbikitsa, monga chifundo, mtendere ndiponso chikondi. Timadziwa kuti kukhala ndi makhalidwe amenewa n’kofunika kwambiri kuti tizisangalatsa Yehova. Timayesetsa kuchotsa mumtima mwathu khalidwe lililonse loipa limene Yesu anachenjeza kuti tizilipewa, monga kupsa mtima. Komanso timapewa maganizo aliwonse oipa, monga okhudza chiwerewere. Timayesetsa kuchita zimenezi chifukwa timadziwa kuti zingatithandize kupewa kuchita tchimo.​—Yakobo 1:14, 15.

Zimene Yesu Ankachita Zinasonyeza Kuti Anali Wanzeru

13, 14. N’chiyani chikusonyeza kuti Yesu anasankha kugwiritsira ntchito moyo wake mwanzeru?

13 Yesu anasonyeza kuti anali wanzeru pa zimene ankalankhula komanso zimene ankachita. Chilichonse pa moyo wake, monga zimene ankasankha kuchita, mmene ankadzionera ndiponso mmene ankachitira zinthu ndi anthu ena, zimasonyeza bwino kwambiri kuti nzeru zake ankazigwiritsa ntchito m’njira zosiyanasiyana. Tiyeni tione zitsanzo zimene zikusonyeza kuti Yesu anali ndi ‘nzeru zopindulitsa ndiponso ankaganiza bwino.’​—Miyambo 3:21.

14 Munthu angasonyeze kuti ndi wanzeru ngati amachita zinthu mozindikira pa moyo wake. Zimene Yesu anasankha kuchita pa moyo wake zimasonyeza kuti ndi wozindikira kwambiri. Iye akanatha kusankha kuti akhale ndi moyo wapamwamba ndiponso kuti akhale ndi zinthu zabwino kwambiri. Mwachitsanzo, akanatha kumanga nyumba yabwino kwambiri, kukhala ndi bizinezi yaikulu kapenanso kukhala wolamulira wotchuka. Koma Yesu ankadziwa kuti kufunitsitsa kukhala ndi zinthu zimenezi ‘n’kwachabechabe ndipo kuli ngati kuthamangitsa mphepo.’ (Mlaliki 4:4; 5:10) Kukhala ndi moyo wofunitsitsa zinthu zimenezi n’kupusa ndiponso kupanda nzeru. Yesu anasankha kuti akhale ndi moyo wosafuna zambiri. Iye analibe cholinga choti akhale ndi ndalama zambiri kapena katundu wambiri. (Mateyu 8:20) Mogwirizana ndi zimene ankaphunzitsa, iye anali ndi diso loyang’ana pa chinthu chimodzi, chomwe chinali kuchita chifuniro cha Mulungu. (Mateyu 6:22) Yesu anasonyeza nzeru pogwiritsa ntchito nthawi komanso mphamvu zake pa zinthu zokhudzana ndi Ufumu, zomwe ndi zofunika kwambiri poyerekezera ndi zinthu zakuthupi. (Mateyu 6:19-21) Choncho iye anatisiyira chitsanzo chabwino choti titsatire.

15. Kodi otsatira a Yesu angasonyeze bwanji kuti ali ndi diso loyang’ana pa Ufumu wa Mulungu wokha, nanga n’chifukwa chiyani ndi nzeru kuchita zimenezi?

15 Otsatira a Yesu masiku ano amaonanso kuti n’chinthu chanzeru kukhala ndi diso loyang’ana pa chinthu chimodzi chomwe ndi Ufumu wa Mulungu. Choncho, iwo amapewa kutenga ngongole zosafunikira zimene zingawabweretsere mavuto. Amapewanso kuda nkhawa kwambiri ndi zinthu zatsiku ndi tsiku zimene zingawawonongere nthawi ndiponso mphamvu zawo. (1 Timoteyo 6:9, 10) Ndipotu ambiri asintha zina ndi zina pa moyo wawo kuti azikhala moyo wosafuna zambiri n’cholinga choti azithera nthawi yambiri mu utumiki wa Chikhristu, ngakhalenso kuyamba utumiki wanthawi zonse. Palibe chinthu chanzeru kwambiri kuposa kuika zinthu za Ufumu pamalo oyamba m’moyo wathu, zimenezi zimatithandiza kuti tikhale osangalala komanso kuti tilandire madalitso ambiri.​—Mateyu 6:33.

16, 17. (a) Kodi Yesu anasonyeza bwanji kuti anali wodzichepetsa komanso kuti ankadziwa kuti pali zinthu zina zimene sangakwanitse kuchita? (b) Kodi tingasonyeze bwanji kuti ndife odzichepetsa komanso kuti tikudziwa kuti pali zinthu zina zimene sitingakwanitse kuchita?

16 Baibulo limasonyeza kuti munthu wanzeru amakhalanso wodzichepetsa. Zimenezi zikutanthauza kuti amazindikira zimene sangakwanitse kuchita. (Miyambo 11:2) Yesu anasonyeza kuti anali wodzichepetsa chifukwa ankadziwa kuti pali zinthu zina zimene sangakwanitse. Iye ankadziwa kuti sakanapangitsa kuti aliyense amene wamva uthenga wake akhale wotsatira wake. (Mateyu 10:32-39) Ankadziwanso kuti anthu amene angakwanitse kuwalalikira ndi ochepa kwambiri. N’chifukwa chake anachita zinthu mwanzeru n’kusiyira otsatira ake ntchito yothandiza anthu kuti akhale ophunzira ake. (Mateyu 28:18-20) Modzichepetsa, Yesu ananena kuti otsatira akewo “adzachita ntchito zazikulu kuposa” zimene iye anachita, chifukwa iwo adzalalikira kwa anthu ambiri, m’madera ambiri ndiponso adzalalikira kwa nthawi yaitali. (Yohane 14:12) Komanso, Yesu sankadziona kuti ndi wapamwamba moti sangathandizidwe ndi wina aliyense. Mwachitsanzo, iye anavomera kuthandizidwa ndi angelo amene anabwera kudzamutumikira pamene anali m’chipululu ndiponso anavomera kuthandizidwa ndi mngelo amene anabwera kudzamulimbikitsa m’munda wa Getsemane. Pa nthawi imene anafunikira kuthandizidwa kwambiri, Mwana wa Mulungu anapemphera mofuula kuti Atate ake amuthandize.​—Mateyu 4:11; Luka 22:43; Aheberi 5:7.

17 Ifenso tiyenera kukhala odzichepetsa ndipo tizidziwa kuti pali zinthu zina zomwe sitingakwanitse. Komabe, tizigwira ndi mtima wonse ntchito yolalikira ndi kuthandiza anthu kuti akhale ophunzira a Yesu ndipo tizichita zimenezi mwakhama kwambiri. (Luka 13:24; Akolose 3:23) Ngakhale zili choncho, tisaiwale kuti Yehova satiyerekezera ndi munthu wina ndipo ifenso tisamachite zimenezi. (Agalatiya 6:4) Nzeru zidzatithandiza kudziikira zolinga zimene tingakwanitsedi zogwirizana ndi mphamvu zathu ndiponso mmene zinthu zilili pa moyo wathu. Komanso, nzeru zingathandize anthu amene ali ndi udindo kuzindikira kuti pali zinthu zina zimene sangakwanitse kuchita pawokha, ndipo angafunike kuthandizidwa ndiponso kulimbikitsidwa nthawi ndi nthawi. Kudzichepetsa kungawathandize kuvomera mwaulemu wina akafuna kuwathandiza ndipo iwo angazindikire kuti Yehova akhoza kugwiritsira ntchito Mkhristu mnzawo kuti ‘awalimbikitse kwambiri.’​—Akolose 4:11.

18, 19. (a) N’chiyani chikusonyeza kuti Yesu anali wololera ndiponso wokoma mtima pochita zinthu ndi ophunzira ake? (b) N’chifukwa chiyani tiyenera kukhala okoma mtima komanso ololera pochita zinthu ndi ena, nanga tingachite bwanji zimenezi?

18 Lemba la Yakobo 3:17 limati: ‘Nzeru yochokera kumwamba ndi yololera.’ Yesu anali wololera ndiponso wokoma mtima pochita zinthu ndi ophunzira ake. Ngakhale kuti ankadziwa zimene ophunzirawo ankalakwitsa, iye ankayang’ana zabwino zimene iwo ankachita. (Yohane 1:47) Yesu ankadziwa kuti ophunzira akewo adzamuthawa usiku umene adzamangidwe, komabe sanakayikire zoti iwo anali okhulupirika. (Mateyu 26:31-35; Luka 22:28-30) Mwachitsanzo, Petulo anakana katatu zoti amamudziwa Yesu. Komabe, Yesu anapempherera Petulo ndipo anasonyeza kuti akudziwa kuti anali wokhulupirika. (Luka 22:31-34) Ndipo usiku womaliza atatsala pang’ono kupita kumwamba, pamene ankapemphera kwa Atate ake, Yesu sanatchule zinthu zimene ophunzira akewo ankalakwitsa. M’malomwake, ananena zinthu zabwino zimene iwo ankachita mpaka usiku umenewu. Yesu anati: “Iwo amvera mawu anu.” (Yohane 17:6) Ngakhale kuti ophunzirawo sanali angwiro, iye anawasiyira ntchito yolalikira za Ufumu wake komanso kuthandiza anthu kuti akhale ophunzira ake. (Mateyu 28:19, 20) Chifukwa chakuti Yesu anasonyeza kuti ankawadalira komanso kuwakhulupirira, n’zosakayikitsa kuti zimenezi zinawalimbikitsa kuti akwanitse kugwira ntchito imene iye anawalamula.

19 Otsatira a Yesu ali ndi zifukwa zomveka zotsanzirira chitsanzo chakechi. Ngati Mwana wa Mulungu yemwe ndi wangwiro, anali woleza mtima pochita zinthu ndi ophunzira ake amene si angwiro, ndiye kuti ifenso omwe ndi anthu ochimwa, tiyenera kukhala oleza mtima pochita zinthu ndi anzathu. (Afilipi 4:5) M’malo momaganizira kwambiri zolakwa za Akhristu anzathu, tingachite bwino kumaona zabwino zimene amachita. Ndipo tizikumbukira kuti Yehova ndi amene anawakoka. (Yohane 6:44) Izitu zikusonyeza kuti Mulungu amaona zabwino zimene iwo amachita ndipo ifenso tizitengera chitsanzo chake. Zimenezi zingatithandize kuti ‘tizinyalanyaza zolakwa’ zawo komanso kuti tizifufuza zabwino zimene abale athuwo amachita n’kumawayamikira. (Miyambo 19:11) Tikamasonyeza kuti abale ndi alongo athu a Chikhristu timawadalira, zimawalimbikitsa kuti azitumikira Yehova ndipo amasangalala ndi utumiki wawo.​—1 Atesalonika 5:11.

20. Kodi tiyenera kuchita chiyani ndi nzeru zakuya zopezeka m’Mauthenga Abwino, ndipo n’chifukwa chiyani tiyenera kuchita zimenezo?

20 Munkhani za m’Mauthenga Abwino, zomwe zimafotokoza za moyo ndi utumiki wa Yesu, timapezamo nzeru zakuya. Kodi tizichita chiyani ndi nzeru zimenezi, zomwe ndi mphatso yamtengo wapatali? Pomaliza ulaliki wake wa paphiri, Yesu analimbikitsa anthu amene ankamvetsera mawu ake anzeruwo kuti azichita kapena kutsatira zimene amvazo, osati kungomvetsera chabe. (Mateyu 7:24-27) Maganizo athu, zolinga zathu komanso zochita zathu zikamagwirizana ndi mawu ndiponso zochita za Yesu zomwe ndi zanzeru, tidzakhala ndi moyo wabwino panopa ndipo tidzapitiriza kuyenda m’njira ya kumoyo wosatha. (Mateyu 7:13, 14) Ndithudi kuchita zimenezi ndi chinthu chabwino kwambiri komanso chanzeru kuposa chilichonse.

a Nkhani imene Yesu anakamba tsiku limenelo ndi imene imadziwika kuti ulaliki wa paphiri. M’Baibulo, nkhaniyi ili pa Mateyu 5:3 mpaka 7:27, ndipo ili ndi mavesi 107. N’kutheka kuti Yesu anakamba nkhaniyi maminitsi pafupifupi 20 okha basi.

b Zikuoneka kuti ‘kumwamba kutatseguka’ pa nthawi ya ubatizo wake, Yesu anakumbukira moyo umene anali nawo kumwambako asanabwere padziko lapansi.​—Mateyu 3:13-17.