Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

MUTU 6

“Anaphunzira Kumvera”

“Anaphunzira Kumvera”

1, 2. N’chifukwa chiyani bambo wachikondi angasangalale kuona mwana wake akumumvera, ndipo kodi zimenezi zikusonyeza bwanji mmene Yehova amamvera?

 TAYEREKEZERANI kuti mukuona bambo akusuzumira pawindo n’kumaonerera mwana wake wamwamuna akusewera mpira ndi anzake. Kenako mpirawo ukugwera mumsewu. Koma mwanayo wangoima n’kumauyang’ana mwachidwi. Ndiyeno mnzake wina akumuuza kuti apite kukautola, koma iye akukana n’kunena kuti: “Bambo anga anandiletsa kusewera mumsewu.” Atamva zimenezi bambowo akumwetulira.

2 N’chifukwa chiyani bambowo akusangalala? Chifukwa chakuti anamuuza mwana wawoyo kuti asamasewere mumsewu. Mwanayo wamvera malangizowo ngakhale kuti sakudziwa kuti bambo akewo akumuona. Bambowo akudziwa kuti mwana wawo akuphunzira kukhala womvera komanso kuti zimenezi zidzamuthandiza kwambiri. Mmene bambowo akumvera mumtima ndi mmenenso Yehova, Atate wathu wakumwamba amamvera. Mulungu akudziwa kuti tiyenera kumukhulupirira komanso kumumvera kuti tikhalebe okhulupirika ndiponso kuti tidzalandire madalitso amene watisungira m’tsogolo. (Miyambo 3:5, 6) Kuti tikwanitse kuchita zimenezi, iye anatitumizira mphunzitsi wabwino kwambiri kuposa munthu aliyense.

3, 4. Kodi mfundo yakuti Yesu “anaphunzira kumvera” ndiponso ‘anakhala wangwiro’ ikutanthauza chiyani? Perekani chitsanzo.

3 Baibulo limatchula mfundo inayake yosangalatsa yokhudza Yesu. Limati: “Ngakhale kuti anali Mwana wa Mulungu, anaphunzira kumvera chifukwa cha mavuto amene anakumana nawo. Ndipo atakhala wangwiro, anali ndi udindo wopulumutsa kwamuyaya anthu onse amene amamumvera.” (Aheberi 5:8, 9) Mwana woyamba kubadwayu anakhalapo kumwamba kwa zaka zambirimbiri ndipo anaona Satana komanso angelo ena akugalukira Mulungu koma iye sanagwirizane nawo. Ponena za iye, ulosi wouziridwa umati: “Ine sindinamupandukire.” (Yesaya 50:5) Ndiye ngati nthawi zonse Yesu amamvera Atate ake n’chifukwa chiyani tikunena kuti “anaphunzira kumvera”? Ngati Yesu anali kale wangwiro n’chifukwa chiyani tikunena kuti ‘anakhala wangwiro’ atabwera padzikoli?

4 Kuti timvetse mfundoyi, tiyerekezere ndi mmisiri womanga nyumba amene akufuna kugula chipangizo chomangira. Iye wagula chipangizo chatsopano chabwino kwambiri. Koma kodi angadziwe bwanji ngati chipangizocho n’cholimba? Ngakhale kuti chipangizocho chikuoneka kuti n’chabwino kwambiri, mmisiriyo angadziwe kuti n’cholimbadi akayamba kuchigwiritsa ntchito kwambiri. N’chimodzimodzi ndi Yesu. Asanabwere padziko lapansi, ankamvera Yehova mokhulupirika. Koma atabwera padziko lapansili anali ndi mwayi woti asonyeze m’njira ina yapadera kuti ndi womvera kwambiri. Iye anakumana ndi mayesero amene sakanakumana nawo akanakhala kumwamba, koma anakhalabe womvera.

5. N’chifukwa chiyani zinali zofunika kwambiri kuti Yesu azimvera Atate wake, nanga kodi m’mutu uno tikambirana chiyani?

5 Yesu anafunikadi kukhala womvera kuti akwaniritse cholinga chimene anabwerera padziko lapansi. Monga “Adamu womalizira,” Yesu anabwera padziko lapansi kudzachita zimene kholo lathu loyamba linalephera kuchita. Iye anamvera Yehova Mulungu ngakhale pamene ankayesedwa. (1 Akorinto 15:45) Komabe sikuti Yesu ankangomvera mokakamizika. Iye ankamvera Mulungu ndi maganizo ake onse, mtima wake wonse komanso moyo wake wonse ndipo ankachita zimenezi mosangalala. Kwa iye, kuchita zimene Atate wake ankafuna chinali chinthu chofunika kwambiri kuposa chakudya. (Yohane 4:34) Kodi chingatithandize n’chiyani kuti tikhale omvera ngati Yesu? Choyamba, tiyeni tione zifukwa zimene zinachititsa Yesu kuti akhale womvera. Ndipo tikakhala ndi zifukwa zofanana ndi za Yesu, tidzatha kupewa mayesero komanso tidzatha kuchita chifuniro cha Mulungu. Tionanso madalitso amene tingapeze tikakhala omvera ngati Khristu.

N’chifukwa Chiyani Yesu Anali Womvera?

6, 7. Kodi zina mwa zifukwa zimene zinachititsa kuti Yesu azimvera Yehova ndi ziti?

6 Yesu anali womvera chifukwa choti anali ndi makhalidwe abwino. Monga mmene tinaonera m’mutu wachitatu, Yesu anali wodzichepetsa. Munthu akakhala wodzikuza safuna kumvera, koma akakhala wodzichepetsa amamvera Yehova ndi mtima wonse. (Ekisodo 5:1, 2; 1 Petulo 5:5, 6) Komanso zinthu zimene Yesu ankakonda ndiponso kudana nazo ndi zimene zinamuthandiza kuti akhale womvera.

7 Chifukwa chachikulu n’chakuti Yesu ankakonda kwambiri Yehova, Atate wake wakumwamba. M’Mutu 13, tidzakambirana za chikondi chimenecho mwatsatanetsane. Chikondi chimenecho n’chimene chinachititsa Yesu kuti aziopa Mulungu. Iye ankaopa kuchita zinthu zimene zingakhumudwitse Yehova, chifukwa chakuti amamukonda komanso kumulemekeza kwambiri. Yesu amaopa Mulungu ndipo zimenezi zinachititsa kuti Mulungu azimva mapemphero ake. (Aheberi 5:7) Panopa Yesu akulamulira monga Mfumu komanso Mesiya ndipo amalamulira mosonyeza kuti amalemekeza Yehova kwambiri ndipo nthawi zonse amafuna kumusangalatsa.​—Yesaya 11:3.

Kodi zosangalatsa zimene mumakonda zimasonyeza kuti mumadana ndi zinthu zoipa?

8, 9. Malinga n’kunena kwa ulosi, kodi Yesu ankaona bwanji chilungamo ndiponso zinthu zoipa, nanga anasonyeza bwanji zimenezo?

8 Munthu amene amakonda Yehova ayeneranso kudana ndi zinthu zimene Yehova amadana nazo. Mwachitsanzo, taonani mawu aulosi otsatirawa okhudza Mesiya yemwenso ndi Mfumu. Mawu ake ndi akuti: “Unkakonda chilungamo ndipo unkadana ndi zoipa. N’chifukwa chake Mulungu, Mulungu wako, wakudzoza ndi mafuta achisangalalo chachikulu kuposa mafumu anzako.” (Salimo 45:7) “Mafumu” ena amene akutchulidwa pa lembali anali ochokera m’banja lachifumu la Mfumu Davide. Pa nthawi imene anadzozedwa, Yesu anali ndi zifukwa zambiri zimene zinamuchititsa kuti asangalale kapena kukondwera kuposa mafumu onsewo. Chifukwa chiyani? Chifukwa chakuti mphoto imene analandira inali yaikulu kuposa mafumu enawo ndipo ufumu wakewo udzabweretsa madalitso ambiri. Yesu analandira mphoto chifukwa chakuti ankamvera Mulungu pa chilichonse. Iye ankamvera Mulungu chifukwa ankakonda chilungamo komanso ankadana ndi zinthu zoipa.

9 Kodi Yesu anasonyeza bwanji kuti amakonda chilungamo ndiponso amadana ndi zoipa? Mwachitsanzo, kodi Yesu anatani otsatira ake atadalitsidwa chifukwa chomvera malangizo ake pa ntchito yolalikira? Iye anasangalala kwambiri. (Luka 10:1, 17, 21) Nanga Yesu anamva bwanji pamene anthu a ku Yerusalemu anasonyeza mobwerezabwereza mtima wosamvera n’kukana zimene iye ankachita pofuna kuwathandiza? Analira chifukwa cha kusamvera kwa anthuwo. (Luka 19:41, 42) Yesu ankakhudzidwa kwambiri ndi zinthu zabwino komanso zoipa zimene anthu ankachita.

10. Kodi timafunika kukhala ndi mtima wotani pa nkhani yokhudza zinthu zabwino ndiponso zoipa, nanga n’chiyani chingatithandize kuchita zimenezo?

10 Tikamaganizira mozama mmene Yesu ankaonera zinthu, zingatithandize kuonanso zimene zimachititsa kuti ifeyo tizimvera Yehova. Ngakhale kuti ndife opanda ungwiro, n’zotheka kuti tizikonda kwambiri zinthu zabwino n’kumadana kwambiri ndi makhalidwe oipa. Tiyenera kupemphera kwa Yehova kuti atithandize kuona zinthu mmene iye ndiponso Mwana wake amaonera. (Salimo 51:10) Komanso tiyenera kupewa zinthu zimene zingatilepheretse kuona zinthu mmene Yehova ndi Mwana wake amazionera. N’zofunika kuti tizisamala kwambiri posankha zinthu zimene timasangalala nazo komanso anthu ocheza nawo. (Miyambo 13:20; Afilipi 4:8) Tikakhala ndi mtima womvera ngati wa Khristu, ndiye kuti sitidzakhala omvera n’cholinga choti anthu atione. Tidzachita zinthu zoyenera chifukwa chakuti timakonda kuchita zinthuzo. Tidzapewa kuchita zinthu zoipa, osati chifukwa choopa kugwidwa, koma chifukwa choti timadana ndi zoipazo.

“Iye Sanachite Tchimo”

11, 12. (a) Kodi n’chiyani chinachitikira Yesu atangoyamba kumene utumiki wake? (b) Kodi poyamba Satana anamuyesa bwanji Yesu, nanga ndi njira ziti zaukathyali zimene anagwiritsa ntchito?

11 Yesu atangoyamba kumene utumiki wake anayesedwa ndipo anasonyeza kuti amadana ndi tchimo. Yesu atabatizidwa anakhala m’chipululu osadya kwa masiku 40, masana ndi usiku. Masiku 40 amenewo atatha Satana anabwera kudzamuyesa. Taonani mmene Mdyerekezi ananenera zinthu mwaukathyali.​—Mateyu 4:1-11.

12 Choyamba Satana ananena kuti: “Ngati ndinu mwana wa Mulungu, uzani miyalayi kuti isanduke mitanda ya mkate.” (Mateyu 4:3) Kodi Yesu anamva bwanji atasala kudya nthawi yaitali? Baibulo limanena momveka bwino kuti: “Anamva njala.” (Mateyu 4:2) Choncho Satana anapezerapo mwayi ndipo mosakayikira anayembekezera mpaka Yesu atafooka ndi njala. Onaninso mawu a mtopola amene Satana ananena. Iye anati: “Ngati ndinu mwana wa Mulungu.” Satana ananena zimenezi ngakhale kuti ankadziwa zoti Yesu ndi “woyamba kubadwa wa chilengedwe chonse.” (Akolose 1:15) Komabe, Yesu sanalole kuti Satana amuchititse kuti asamvere Mulungu. Yesu ankadziwa kuti si cholinga cha Mulungu kuti iye agwiritse ntchito mphamvu zake ndi zolinga zolakwika. Iye anakana kuchita zofuna za Satana ndipo anasonyeza kuti ankadalira kwambiri Yehova kuti amupatse chakudya komanso kumutsogolera.​—Mateyu 4:4.

13-15. (a) Kodi Satana anamuyesa bwanji Yesu kachiwiri ndi kachitatu, nanga Yesu anachita chiyani? (b) Kodi tikudziwa bwanji kuti Yesu ankakhala tcheru nthawi zonse polimbana ndi Satana?

13 Pamene Satana ankayesa Yesu kachiwiri, anamutenga n’kupita naye pamwamba pa khoma la mpanda wa kachisi. Mochenjera kwambiri, Satana anapotoza Mawu a Mulungu poyesa Yesu kuti achite zinthu modzionetsera. Iye anamuuza kuti adziponye pansi kuti angelo amupulumutse. Gulu la anthu amene anali pakachisipo akanaona zodabwitsazo, kodi pakanapezeka aliyense wokayikira zoti Yesu anali Mesiya wolonjezedwa? Ngati anthuwo akanavomereza kuti iye ndi Mesiya chifukwa cha zodabwitsazo, kodi zimenezi sizikanachititsa kuti Yesu asakumane ndi mavuto ambiri? Mwina zikanaterodi. Koma Yesu ankadziwa kuti Yehova akufuna kuti Mesiya agwire ntchito yake modzichepetsa, osati kuchita zinthu zodabwitsa modzionetsera kuti anthu amukhulupirire. (Yesaya 42:1, 2) Choncho Yesu anakananso kuchita zinthu zosonyeza kusamvera Yehova ndipo sanakodwe ndi msampha wofuna kutchuka.

14 Koma kodi Yesu anakodwa ndi msampha woti akhale wolamulira? Pamene ankamuyesa kachitatu, Satana anauza Yesu kuti amupatsa maufumu onse a padziko lapansi ngati atamulambira kamodzi kokha. Kodi iye anayamba waganizira kaye zimene Satana anamuuzazo? Ayi, chifukwa nthawi yomweyo anamuyankha kuti: “Choka Satana! Chifukwa Malemba amati, ‘Yehova Mulungu wako ndi amene uyenera kumulambira ndipo uyenera kutumikira iye yekha basi.’” (Mateyu 4:10) Palibe chimene chikanakopa Yesu kuti alambire mulungu wina, n’kuchita zinthu zosonyeza kusamvera Yehova chifukwa chofuna kukhala wolamulira kapena wotchuka m’dzikoli.

15 Kodi Satana analekera pomwepo? N’zoona kuti Yesu atamulamula kuti achoke, anachokadi. Koma Uthenga Wabwino wa Luka umanena kuti Mdyerekezi “anamusiya mpaka nthawi ina yabwino.” (Luka 4:13) Ndithudi, pa nthawi yonse imene Yesu anali padziko lapansi, Satana anapitiriza kumuyesa pa mpata uliwonse umene anapeza. Baibulo limanena kuti Yesu “anayesedwa pa zinthu zonse.” (Aheberi 4:15) Izi zikusonyeza kuti Yesu ankakhala tcheru nthawi zonse ndipo ifenso tizichita chimodzimodzi.

16. Kodi Satana amayesa bwanji atumiki a Mulungu masiku ano, nanga tingapewe bwanji misampha yake?

16 Masiku ano Satana akupitiriza kuyesa atumiki a Mulungu. N’zomvetsa chisoni kuti iye amatipezerera chifukwa chakuti si ife angwiro. Mwachibadwa, anthufe timakhala ndi mtima wodzikonda, wodzikuza ndiponso wofuna kulamulira ena ndipo Satana amapezerapo mwayi n’kumatiyesa. Iye angagwiritse ntchito makhalidwe onsewa nthawi imodzi kuti atikole mumsampha wokonda chuma. Choncho m’pofunika kuti nthawi ndi nthawi tizidzifufuza moona mtima. Tiyenera kumaganizira mozama mawu opezeka pa 1 Yohane 2:15-17. Tikamachita zimenezi, tingachite bwino kudzifufuza kuti tione ngati kufuna kuchita zinthu za m’dzikoli, kufunitsitsa kukhala ndi chuma, kapena kufunitsitsa kuchita zinthu zogometsa anthu, zikuchititsa kuti tisiye kukonda kwambiri Atate wathu wakumwamba. Tizikumbukira kuti dzikoli likupita limodzi ndi Satana amene ndi wolamulira wake. Choncho tisalole kuti atikope kuti tichite tchimo. Tiyeni tizitsanzira Ambuye wathu amene “sanachite tchimo.”​—1 Petulo 2:22.

“Ndimachita Zinthu Zimene Zimamusangalatsa Nthawi Zonse”

17. Kodi Yesu ankaona bwanji nkhani yomvera Atate ake, nanga anthu ena anganene kuti chiyani?

17 Pali zambiri zimene munthu ayenera kuchita posonyeza kuti ndi womvera osati kungopewa tchimo lokha. Mwachitsanzo, Khristu ankachita ndi mtima wonse zinthu zonse zimene Atate ake ankamulamula. Iye anati: “Ndimachita zinthu zimene zimamusangalatsa nthawi zonse.” (Yohane 8:29) Yesu ankakhala wosangalala kwambiri chifukwa choti anali womvera. Anthu ena anganene kuti zinali zosavuta kuti Yesu asonyeze kuti ndi womvera tikayerekezera ndi ife. Iwo anganene kuti Yesu ankangofunikira kumvera Yehova yekha, yemwe ndi wangwiro, pamene anthufe timafunikira kumvera anthu anzathu omwe si angwiro amene ali ndi udindo. Koma zoona zake n’zakuti Yesu ankamveranso anthu omwe si angwiro amene anali ndi maudindo.

18. Pamene anali wachinyamata, kodi Yesu anapereka chitsanzo chotani pa nkhani yomvera?

18 Yesu anakulira m’banja la Yosefe ndi Mariya, amene anali makolo omwe si angwiro. Ndipo kuposa mwana aliyense, iye ankaona kwambiri zimene makolo akewo ankalakwitsa. Kodi iye anasiya kumvera makolo akewo n’kuyamba kuwalangiza mmene angayendetsere banjalo? Taonani zimene lemba la Luka 2:51 limanena zokhudza Yesu ali ndi zaka 12. Lembali limati: “Anapitiriza kuwamvera.” Pamenepa Yesu anapereka chitsanzo chabwino kwa achinyamata a Chikhristu, amene amayesetsa kumvera makolo awo ndiponso kuwalemekeza.​—Aefeso 6:1, 2.

19, 20. (a) Kodi Yesu anakumana ndi mavuto otani pa nkhani yomvera anthu omwe si angwiro? (b) N’chifukwa chiyani Akhristu masiku ano ayenera kumvera anthu amene akuwatsogolera?

19 Pa nkhani yomvera anthu omwe si angwiro, Yesu anakumana ndi mavuto amene Akhristu oona masiku ano sangakumane nawo. Taganizirani mmene zinthu zinalili pa nthawiyo. Kwa nthawi yaitali, Yehova ankasangalala ndi chipembedzo cha Ayuda. Iwo anali ndi kachisi ku Yerusalemu ndipo ansembe ankatumikira m’kachisimo. Koma tsopano Yehova anali atatsala pang’ono kuchotsa chipembedzo chimenecho kuti akhazikitse mpingo wa Chikhristu. (Mateyu 23:33-38) Pa nthawiyi atsogoleri ambiri achipembedzo ankaphunzitsa zinthu zabodza zimene Agiriki ankakhulupirira. Anthu ankachita zinthu zambiri zachinyengo m’kachisi moti Yesu anatchula kachisiyo kuti ndi “phanga la achifwamba.” (Maliko 11:17) Kodi Yesu anasiya kupita kukachisiko ndi kumasunagoge? Ayi, chifukwa chakuti Yehova ankagwiritsabe ntchito zinthu zimenezo. Yesu anasonyeza kuti ndi womvera ndipo ankapitabe ku zikondwerero za kukachisi komanso ankapita kusunagoge mpaka pamene Mulungu anasintha zinthu.​—Luka 4:16; Yohane 5:1.

20 Popeza kuti Yesu anakhalabe womvera ngakhale kuti zinthu zinali choncho, nawonso Akhristu oona masiku ano ayenera kukhala omvera. Ndipotu zinthu masiku ano n’zosiyana ndi mmene zinalili m’nthawi ya Yesu. Mogwirizana ndi ulosi, ife tikukhala m’nthawi imene kulambira koyera kwabwezeretsedwa. Mulungu akutilonjeza kuti sadzalola kuti Satana asokoneze anthu amene akumulambira m’njira yovomerezeka. (Yesaya 2:1, 2; 54:17) N’zoona kuti mumpingo wa Chikhristu nthawi zina anthu amachimwa komanso kuchita zinthu zosayenera chifukwa choti si angwiro. Koma kodi tizisiya kumvera Yehova, mwina mpaka kusiya kupita kumisonkhano ya Chikhristu kapena kuyamba kunyoza akulu chifukwa cha zolakwa za anthu ena? Ayi ndithu. M’malomwake, timamvera ndi mtima wonse abale amene akutitsogolera mumpingo. Timasonyeza kuti ndife omvera tikamapita kumisonkhano ya Chikhristu ndiponso tikamagwiritsa ntchito mfundo za m’Malemba zimene timaphunzira kumisonkhanoko.​—Aheberi 10:24, 25; 13:17.

Timasonyeza kumvera tikamagwiritsa ntchito zimene timaphunzira kumisonkhano ya Chikhristu

21. Kodi Yesu anatani anthu atamulimbikitsa kuti achite zinthu zosonyeza kusamvera Mulungu, ndipo anatipatsa chitsanzo chotani?

21 Yesu sanalole anthu ena, ngakhale anzake amene anali ndi zolinga zabwino, kuti amulepheretse kumvera Yehova. Mwachitsanzo, mtumwi Petulo anayesa kulimbikitsa Ambuye wake kuti asalole kuti avutike ndiponso kufa. Ngakhale kuti Petulo anali ndi zolinga zabwino pamene ankalankhula zimenezi, Yesu anakana malangizo olakwika akuti adzikomere mtima. (Mateyu 16:21-23) Masiku ano, otsatira a Yesu kawirikawiri amapewa kukopedwa ndi achibale amene akuwalimbikitsa kuti asiye kumvera malamulo ndi mfundo za Mulungu. Mofanana ndi otsatira a Yesu oyambirira, ifenso timatsatira mfundo yakuti “tiyenera kumvera Mulungu monga wolamulira, osati anthu.”​—Machitidwe 5:29.

Tikakhala Omvera Ngati Khristu Tidzapeza Madalitso

22. Kodi Yesu anapereka yankho la funso liti, nanga analipereka bwanji?

22 Sizinali zophweka kuti Yesu akhalebe womvera pamene anamugwira kuti akamuphe. Koma pa tsiku lovutali, “anaphunzira kumvera” kwambiri. Iye anachita zimene Atate wake ankafuna osati zofuna zake. (Luka 22:42) Pochita zimenezi, anasonyeza mwapadera kwambiri kuti n’zotheka kutumikira Mulungu mokhulupirika. (1 Timoteyo 3:16) Iye anapereka yankho la funso limene lakhalapo kwa nthawi yaitali lakuti: Kodi munthu wangwiro angakhalebe womvera kwa Yehova ngakhale pamene akuyesedwa? Adamu ndi Hava analephera kukhalabe omvera. Koma kenako Yesu anabwera ndipo anasonyeza kuti n’zotheka munthu kukhalabe wokhulupirika mpaka imfa. Mwana wa Mulungu, yemwe ndi munthu wapamwamba kwambiri kuposa zolengedwa zonse za Yehova, anapereka yankho lamphamvu kwambiri. Iye anakhalabe womvera ngakhale kuti anavutika mpaka imfa.

23-25. (a) Kodi kumvera n’kogwirizana bwanji ndi kukhala wokhulupirika? Perekani chitsanzo. (b) Kodi m’mutu wotsatira tikambirana chiyani?

23 Tikakhala omvera timasonyeza kuti ndife odzipereka kwa Yehova ndi mtima wonse ndiponso kuti tikumutumikira mokhulupirika. Chifukwa chokhalabe womvera, Yesu anasonyeza kuti amatumikira Mulungu mokhulupirika ndipo zimenezi zinathandiza anthu onse. (Aroma 5:19) Yehova anadalitsa kwambiri Yesu ndipo ifenso adzatidalitsa tikamamvera Khristu, Ambuye wathu. Tikamamvera Khristu ‘tidzapulumutsidwa kwamuyaya.’​—Aheberi 5:9.

24 Kuwonjezera pamenepo, anthu amene amatumikira Mulungu mokhulupirika amadalitsidwa. Lemba la Miyambo 10:9 limati: “Munthu wochita zinthu mokhulupirika adzakhala wotetezeka.” Kukhala wokhulupirika tingakuyerekezere ndi nyumba yaikulu imene anaimanga ndi njerwa ndipo chilichonse chimene tachita posonyeza kuti ndife omvera tingachiyerekezere ndi njerwa imodzi. Njerwa imodzi ingaoneke ngati yopanda ntchito, koma kwenikweni njerwa iliyonse ndi yofunika. Ndipo tikasanja njerwa zambirimbiri pomanga nyumba, pamapeto pake imakhala nyumba yokongola kwambiri. N’chimodzimodzinso ndi kutumikira Mulungu mokhulupirika. Tikamachita zinthu zosiyanasiyana zosonyeza kumvera tsiku ndi tsiku komanso chaka ndi chaka, zinthu zonsezo kuziphatikiza pamodzi zimatithandiza kuti tikhale anthu okhulupirika.

25 Munthu akakhala womvera kwa nthawi yaitali ndiye kuti ali ndi khalidwe lina labwino lomwe ndi kupirira. M’mutu wotsatira tikambirana mmene Yesu anasonyezera khalidwe limeneli.