Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

MUTU 109

Anadzudzula Atsogoleri Achipembedzo Omwe Ankamutsutsa

Anadzudzula Atsogoleri Achipembedzo Omwe Ankamutsutsa

MATEYU 22:41–23:24 MALIKO 12:35-40 LUKA 20:41-47

  • KODI KHRISTU NDI MWANA WA NDANI?

  • YESU ANANENA POYERA KUTI ANTHU AMENE ANKAMUTSUTSA ANALI ACHINYENGO

Atsogoleri achipembedzo analephera kuchititsa Yesu manyazi komanso analephera kumugwira kuti akamupereke kwa Aroma. (Luka 20:20) Ndiyeno pa Nisani 11, Yesu ali kukachisi anthu omwe ankamutsutsa anabwera kuti adzamukole mawu koma zinthu zinatembenuka. Yesu ndi amene anayamba kuwapanikiza ndipo ananena poyera kuti iyeyo ndi Mesiya. Iye anawafunsa kuti: “Mukuganiza bwanji za Khristu? Kodi ndi mwana wa ndani?” (Mateyu 22:42) Anthu ankadziwa kuti Khristu kapena kuti Mesiya adzachokera mumzera wa Davide ndipo ndi zimene anthuwo anayankha Yesu.—Mateyu 9:27; 12:23; Yohane 7:42.

Yesu anawafunsanso kuti: “Nanga n’chifukwa chiyani mouziridwa ndi mzimu, Davide anamutcha ‘Ambuye,’ muja anati, ‘Yehova wauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja kufikira nditaika adani ako kunsi kwa mapazi ako”’? Chotero ngati Davide anamutcha kuti ‘Ambuye,’ akukhala bwanji mwana wake?”—Mateyu 22:43-45.

Afarisiwo sanayankhe chifukwa ankayembekezera kuti munthu wochokera mumzera wa Davide ndi amene adzawalanditse ku ulamuliro wa Aroma. Ndiyeno Yesu anagwiritsa ntchito mawu amene Davide ananena pa Salimo 110:1, 2 pofuna kusonyeza kuti Mesiya sadzakhala wolamulira wamba. Yesu anafotokoza kuti Mesiya ndi Mbuye wa Davide ndipo adzayamba kugwiritsa ntchito mphamvu zake akadzakhala kudzanja lamanja la Mulungu. Zimene Yesu anawayankha zinawasowetsa chonena.

Pa nthawi imene Yesu ankalankhula zimenezi, ophunzira ake komanso anthu ena ankangomvetsera. Ndiyeno Yesu anayamba kulankhula nawo ndipo anawachenjeza za alembi ndi Afarisi. Yesu anawauza kuti anthu amenewa “adzikhazika pampando wa Mose” kuti aziphunzitsa anthu Chilamulo cha Mulungu. Yesu anauza anthuwo kuti: “Muzichita ndi kutsatira zilizonse zimene angakuuzeni, koma musamachite zimene iwo amachita, chifukwa iwo amangonena koma osachita.”—Mateyu 23:2, 3.

Kenako Yesu anafotokoza zinthu zomwe zinasonyeza kuti alembi ndi Afarisi anali achinyengo. Iye anati: “Iwo amakulitsa timapukusi tokhala ndi malemba timene amavala monga zodzitetezera.” Ayuda ena ankavala timapukusi tomwe tinkaoneka ngati kabokosi kakang’ono pachipumi kapena padzanja ndipo tinkakhala ndi mawu a m’Chilamulo. Koma Afarisi ankavala timapukusi tatikulu kuposa timeneti pofuna kusonyeza anthu kuti iwo anali odzipereka kwambiri potsatira Chilamulo. Afarisiwa ‘ankakulitsanso ulusi wopota wa m’mphepete mwa zovala zawo.’ Aisiraeli ankafunika kuika ulusi wopota m’mphepete mwa zovala zawo, koma Afarisi ankawonetsetsa kuti ulusi wa zovala zawo uzikhala wautali kwambiri. (Numeri 15:38-40) Ankachita zimenezi “kuti anthu awaone.”—Mateyu 23:5.

Yesu ankadziwanso kuti ophunzira ake akhoza kutengera mtima wofuna kukhala otchuka, choncho anawalangiza kuti: “Koma inu musamatchulidwe kuti Rabi, chifukwa mphunzitsi wanu ndi mmodzi yekha, ndipo nonsenu ndinu abale. Komanso musamatchule aliyense kuti atate wanu padziko lapansi pano, pakuti Atate wanu ndi mmodzi, wakumwamba Yekhayo. Musamatchedwe ‘atsogoleri,’ pakuti Mtsogoleri wanu ndi mmodzi, Khristu.” Ndiye ophunzirawo ankayenera kudziona bwanji, nanga ankafunika kuchita bwanji zinthu ndi anthu ena? Yesu anawauza kuti: “Koma wamkulu kwambiri pakati panu akhale mtumiki wanu. Aliyense wodzikweza adzatsitsidwa, koma aliyense wodzichepetsa adzakwezedwa.”—Mateyu 23:8-12.

Kenako Yesu ananena zimene zidzachitikire alembi ndi Afarisi achinyengowo. Iye anati: “Tsoka kwa inu alembi ndi Afarisi, onyenga inu! Chifukwa mukutseka ufumu wakumwamba kuti anthu asalowemo. Pakuti inuyo simukulowamo, mukuletsa amene akufuna kulowamo kuti asalowe.”—Mateyu 23:13.

Yesu anadzudzula Afarisi chifukwa chakuti sankaona zinthu zofunika ngati mmene Yehova amazionera ndipo zimenezi zinkaonekera pa malamulo osamveka amene iwo ankaika. Mwachitsanzo, iwo ankanena kuti: “Ngati munthu walumbirira kachisi palibe kanthu, koma ngati munthu walumbirira golide wa m’kachisi, asunge lumbiro lake.” Iwo ankasonyeza kuti anali okonda chuma chifukwa ankaganizira kwambiri za golide wa m’kachisi m’malo moganizira kuti kachisiyo ndi malo amene ankalambirirako Yehova. Komanso ‘ankanyalanyaza zinthu zofunika za m’Chilamulo, monga chilungamo, chifundo ndi kukhulupirika.”—Mateyu 23:16, 23; Luka 11:42.

Yesu ananena kuti Afarisiwa anali ‘atsogoleri akhungu, amene ankasefa zakumwa zawo kuti achotsemo kanyerere koma ankameza ngamila.’ (Mateyu 23:24) Afarisi ankasefa vinyo wawo kuti achotsemo nyerere chifukwa nyerereyo inali m’gulu la tizilombo todetsedwa. Koma chifukwa chakuti ankanyalanyaza zinthu zofunika kwambiri za m’Chilamulo, zinali ngati kuti akumeza ngamila yomwenso inali nyama yodetsedwa.—Levitiko 11:4, 21-24.