Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Anthu Ambiri Adzapita—Nanga Inu Bwanji?

Anthu Ambiri Adzapita—Nanga Inu Bwanji?

Anthu Ambiri Adzapita—Nanga Inu Bwanji?

Adzapita kuti? Kumwambo wapachaka wokumbukira imfa ya Yesu Kristu. Chaka chatha, amene anasonkhana pamwambo umenewu padziko lonse anakwana 14,872, 086.

Kodi anthu amapitiranji kumwambowu? Chifukwa cha zimene imfa ya Kristu idzachitire mtundu wa anthu. Posachedwapa idzabweretsa mpumulo, idzachotsa matenda, kuvutika ndi imfa. Ngakhale anthu amene tinkawakonda omwe anamwalira adzaukitsidwa kukhala amoyo padziko lapansi la Paradaiso.

Kodi imfa ya Yesu ingadzabweretse motani madalitso ameneŵa? Fufuzani. Mboni za Yehova zikukuitanani kuti mudzachite nawo mwambo wofunika umenewu.

Dzapiteni ku Nyumba ya Ufumu yapafupi ndi kwanu. Chaka chino mwambowu udzachitika pa April 8, Lamlungu dzuŵa litaloŵa. Funsani Mboni za Yehova kwanuko nthaŵi yake yeniyeni.