Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Pamene Panayambira Nkhaniyi

Pamene Panayambira Nkhaniyi

Pamene Panayambira Nkhaniyi

TAUNI ya stratton, yomwe ili m’boma la ohio, ku united states ndi tauni yaing’ono imene ili pafupi ndi mtsinje wa Ohio, womwe uli malire a boma la Ohio ndi West Virginia. Tauniyi ili ndi anthu osakwana 300 ndipo ili ndi meya wake. Mu 1999 zinthu zinavuta m’tauniyi pamene akuluakulu a tauniyi anafuna kukhazikitsa lamulo loti anthu azikatenga kaye chilolezo kuboma akamayendera ena m’makomo. Lamuloli linakhudza Mboni za Yehova chifukwa cha ntchito yawo youza ena uthenga wa m’Baibulo.

Moti pamenepa pali nkhani? Inde, ndipo muona m’nkhani inoyo kuti kwenikweni boma litati likhazikitse lamulo lotere, Mboni za Yehova komanso anthu ena onse okhala ku United States sangamayankhule ndi ena mwaufulu.

Chimene Chinatsitsa Dzaye

Mboni za Yehova za mumpingo wa Wellsville m’tauni ya Stratton zakhala zikuchezera anthu a m’tauniyi kuyambira kalekale ndipo kungoyambira mu 1979 akuluakulu ena a kumeneko akhala akuzivutitsa chifukwa cha utumiki wawo wa kunyumba ndi nyumba. Kumayambiriro kwa m’ma 1990, wapolisi wina kumeneku anapirikitsa Mboni zina m’tauniyi, amvekere: “Zipitani; zaufulu wanuzo ine ndilibe nazo ntchito.”

Komano nkhaniyi inafika pachiindeinde mu 1998 pamene meya weniweniyo anapezeketsa a Mboni za Yehova anayi. Iwo ankatuluka m’tauniyo pagalimoto yawo atachezamo ndi anthu ena amene anali ndi chidwi chokambirana za m’Baibulo. M’modzi wa azimayi amene anawapezeketsawo anati meyayo anawauza kuti bwenzi atawamangitsa kungoti achita mwayi poti si azibambo.

Koma chimene chinabutsa nkhani yaposachedwapa ndi lamulo la tauniyi loletsa kupempha zinthu ndiponso kutsatsa malonda m’makomo mwa eniake popanda eniakewo kukuitanani. Lamuloli n’lakuti aliyense wofuna kuyenda khomo ndi khomo ayenera kukatenga kaye chilolezo kwa meya ndipo n’chaulere. Koma Mboni za Yehova zinaona kuti lamulo lotere n’loletsa anthu kuyankhulana, kupembedza, ndiponso kufalitsa nkhani mwaufulu. Motero tauniyi itakana kusintha lamuloli anaidulira chisamani ku khoti la m’bomalo.

Pa July 27, 1999, jaji wamkulu wa khoti la kum’mwera kwa boma la Ohio anazenga mlanduwu. Iye anagamula kuti lamulo la tauniyo n’logwirizana ndi malamulo aboma. Kenaka pa February 20, 2001, khoti la apilo ku America linaugamulanso chimodzimodzi mlanduwu.

Pofuna kuthetseratu nkhaniyi, bungwe la Watchtower Bible and Tract Society of New York mogwirizana ndi mpingo wa Mboni za Yehova m’tauniyi wotchedwa Wellsville anapempha kuti a khoti lalikulu kwambiri ku America auonenso mlanduwu.

[Mapu/Chithunzi patsamba 3]

(Onani m’magazini yeniyeni kuti mumvetse izi)

Los Angeles

New York

OHIO

Stratton