Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Chifukwa Chimene Timakhulupirira Kuti Kuli Mlengi

Chifukwa Chimene Timakhulupirira Kuti Kuli Mlengi

Chifukwa Chimene Timakhulupirira Kuti Kuli Mlengi

Akatswiri ambiri a zinthu zosiyanasiyana amatha kuona kuti pali winawake amene analenga zamoyo. Amaona kuti si zomveka kunena kuti zinthu zamoyo zopangidwa mwaluso zomwe zili padziko lapansi zinangokhalapo mwangozi. Choncho, asayansi ndi ochita kafukufuku angapo amakhulupirira kuti Mlengi alipo.

Ena mwa amenewa panopa ndi Mboni za Yehova. Amakhulupirira kuti Mulungu wotchulidwa m’Baibulo ndi amene anapanga zinthu zopezeka m’chilengedwe chonse. Kodi afika pokhulupirira zimenezi chifukwa chiyani? Olemba Galamukani! anafunsa ena a iwo kuti apereke zifukwa zake. Mukhoza kusangalala kumva zimene ananena. *

“Zinthu Zovuta Kumvetsa Zokhudza Moyo”

WOLF-EKKEHARD LÖNNIG

MBIRI YANGA: Pa zaka 28 zapitazi, ndakhala ndikugwira ntchito yasayansi yokhudzana ndi kusintha kwa maselo a zomera. Pa zaka 21 mwa zaka zimenezo, ndinalembedwa ntchito ndi bungwe la Max Planck Institute for Plant Breeding Research, ku Cologne, m’dziko la Germany. Kwa zaka pafupifupi 30 zapitazi, ndakhalanso ndikutumikira monga mkulu mu mpingo wachikristu wa Mboni za Yehova.

Kafukufuku amene ndachita wokhudza chibadwa cha zinthu zamoyo ndi maphunziro anga a sayansi yosiyanasiyana ya zamoyo, monga kagwiridwe ntchito ka ziwalo za zinthu zamoyo ndi kaonekedwe ka zinyama ndi zomera, andichititsa kuzindikira zinthu zochuluka ndiponso zovuta kumvetsa zokhudza moyo. Kuphunzira zinthu zimenezi kwanditsimikizira kuti zamoyo, ngakhale zamoyo zotsika zambiri, ziyenera kuti zinachita kupangidwa ndi winawake wanzeru.

Anthu asayansi akudziwa bwino zinthu zochititsa kaso zopezeka m’zamoyo. Koma mfundo zochititsa kasozi nthawi zambiri amazifotokoza mozigwirizanitsa kwambiri ndi chisinthiko. Komabe ineyo ndimaona kuti mfundo zotsutsana ndi nkhani ya m’Baibulo yonena za kulengedwa kwa zinthu, n’zosamveka tikaziunika mwasayansi. Ndafufuza mfundo zoterozo kwa zaka makumi angapo. Ndaphunzira zambiri zokhudza zinthu zamoyo ndipo ndaganizira mwakuya za mmene malamulo olamulira chilengedwe chonse alili. Ndaona kuti malamulo amenewa amaoneka kuti anakonzedwa m’njira yabwino kwambiri yothandiza kuti padziko lapansi pakhale zamoyo. Chifukwa chochita zimenezi, ndine wotsimikiza kuti Mlengi alipo.

“Chilichonse Chomwe Ndaonapo Chimakhala ndi Chochititsa”

BYRON LEON MEADOWS

MBIRI YANGA: Ndimakhala ku United States ndipo ndimagwira ntchito ku bungwe la National Aeronautics and Space Administration. Ntchito yanga imakhudzana ndi sayansi ya kuwala. Panopa ndikugwira nawo ntchito yofufuza luso latsopano lomwe lingatithandize kuunika bwino nyengo yapadziko lonse, kusinthasintha kwa nyengo m’madera osiyanasiyana ndi zinthu zina zochitika m’mapulaneti. Ndine mkulu mu mpingo wa Mboni za Yehova ku Kilmarnock, m’dera la ku Virginia.

Pa kafukufuku wanga, nthawi zambiri ndimagwiritsa ntchito mfundo za sayansi ya kapangidwe ka zinthu. Ndimayesetsa kumvetsa chifukwa chomwe zinthu zimachitika ndi njira yomwe zimachitikira. Mu ntchito yanga, ndimaona umboni wochita kuonekeratu wosonyeza kuti chilichonse chomwe ndaonapo chimakhala ndi chochititsa. Ndimakhulupirira kuti n’zogwirizana ndi sayansi kukhulupirira kuti Mulungu ndi amene anayambitsa zinthu zonse zamoyo. Malamulo amene zamoyo zimayendera ndi okhazikika bwino kwambiri moti ndimakhulupirira kuti anakhazikitsidwa ndi Mlengi wodziwa kulongosola zinthu.

Ngati mfundo imeneyi ndi yochita kuonekeratu bwino chonchi, n’chifukwa chiyani asayansi ambiri amakhulupirira chisinthiko? Kodi n’kutheka kuti anthu okhulupirira chisinthiko amaona umboni umene ulipo ali kale ndi maganizo ena? Zimenezi si zachilendo pakati pa anthu asayansi. Komabe, ngakhale munthu aone umboni wa zinazake, ngakhale utakhala wotsimikizirika, sizikutanthauza kuti afika pa mfundo yomwe umboniwo ukusonyeza. Mwachitsanzo, munthu amene akufufuza sayansi ya kuwala akhoza kulimbikira kunena kuti kuwala kumayenda ngati mafunde, mofanana ndi momwe phokoso limayendera, chifukwa choti kuwala nthawi zambiri kumachita zinthu ngati mafunde. Komabe, mfundo yakeyo ikhoza kukhala yoperewera chifukwa choti umboni umene ulipo umasonyezanso kuti kuwala kumachita zinthu mofanana ndi gulu la tizinyenyetswa ting’onoting’ono tapadera. Mofanana ndi zimenezi, anthu amene amalimbikira kunena kuti chisinthiko chinachitikadi amatero pongoona umboni wochepa chabe, ndipo amalola kuti maganizo amene ali nawo kale akhudze momwe akuuonera umboniwo.

Zimandidabwitsa kwambiri kuti munthu angakhulupirire kuti chisinthiko chinachitikadi pamene anthu amene amatchedwa akatswiri a chisinthiko amatsutsana okhaokha akamafotokoza momwe chisinthikocho chinachitikira. Mwachitsanzo, kodi mungakhulupirire kuti masamu ndi oona ngati akatswiri ena amanena kuti 2 kuphatikiza 2 yankho lake ndi 4, pamene akatswiri ena akuti yankho lake ndi 3 kapenanso 6? Ngati sayansi imavomereza zinthu zokhazo zomwe tingathe kuzitsimikizira ndi umboni, kuzifufuza, ndi kuzichitanso, ndiye kuti chiphunzitso choti zamoyo zonse zinasinthika kuchokera ku kholo limodzi sichogwirizana ndi sayansi.

“Chinthu Sichingachokere ku Chinthu Chomwe Kulibe”

KENNETH LLOYD TANAKA

MBIRI YANGA: Ndine katswiri wa sayansi ya nthaka ndipo panopa ndikugwira ntchito ku bungwe lofufuza za miyala ku United States lomwe lili mu mzinda wa Flagstaff, ku Arizona. Kwa zaka pafupifupi 30, ndachita nawo kafukufuku wa mbali zosiyanasiyana za sayansi ya nthaka, kuphatikizapo nthaka za mapulaneti ena. Nkhani zambirimbiri za kafukufuku wanga ndi mapu a nthaka ya ku Mars amene ndinalemba zatulutsidwa m’magazini asayansi otchuka. Monga mmodzi wa Mboni za Yehova, ndimatha maola 70 mwezi uliwonse ndikulimbikitsa anthu kuwerenga Baibulo.

Ndinaphunzitsidwa kuti ndizikhulupirira chisinthiko, koma sindikanatha kuvomereza kuti mphamvu zazikulu zomwe zinafunika kuti chilengedwe chonse chipangike zinangoyambika zokha popanda Mlengi wamphamvu. Chinthu sichingachokere ku chinthu chomwe kulibe. Ndimaonanso umboni waukulu woti kuli Mlengi m’Baibulo mwenimwenimo. Buku limeneli lili ndi zitsanzo zambiri za mfundo zogwirizana ndi sayansi imene ineyo ndikudziwa, monga mfundo yoti dziko lapansi n’lozungulira ndi kuti lalenjekeka “pachabe.” (Yobu 26:7; Yesaya 40:22) Mfundo zoona zimenezi zinalembedwa m’Baibulo kalekale, anthu asanazitulukire.

Taganizirani momwe anthufe tinapangidwira. Timatha kumva, kuona, kununkhiza, kulawa, ndiponso kukhudza. Timatha kuchita manyazi, timatha kuganiza zinthu zanzeru, timatha kulankhulana, ndiponso timatha kukhudzidwa mtima. Koposa zonse, timatha kumva kuti tikukondedwa, kuyamikira wina akatisonyeza chikondi, ndi kukonda anthu ena. Chisinthiko sichingafotokoze komwe kunachokera makhalidwe odabwitsa amenewa a anthu.

Dzifunseni kuti, ‘Kodi mfundo zimene amagwiritsa ntchito pophunzitsa chisinthiko zimachokera ku magwero odalirika bwanji?’ Umboni wa zinthu za mu nthaka ndi wosakwanira, wovuta kumvetsa, ndiponso wosokoneza. Anthu okhulupirira chisinthiko alephera kugwiritsa ntchito njira zasayansi kuti asonyeze momwe chisinthiko chinachitikira. Ndipo ngakhale kuti asayansi nthawi zambiri amagwiritsa ntchito luso labwino lochitira kafukufuku, nthawi zambiri amamasulira zinthu zomwe apezazo mogwirizana ndi zolinga zawo. Zinthu zimene apeza zikakhala kuti n’zosakwanira kapena zosemphana ndi zina, asayansi ena apezeka kuti amapititsa patsogolo maganizo awo. Kufuna kupititsa patsogolo ntchito yawo ndi mmene amadzionera iwo eni, zimakhudza kwambiri kachitidwe kawo ka zinthu.

Monga wasayansi komanso wophunzira Baibulo, ndimafufuza choonadi chonse, chimene chimagwirizana ndi mfundo zonse zodziwika ndi zomwe zafufuzidwapo, kuti ndifike pomvetsa zinthu molondola kwambiri. Ine ndimaona kuti kukhulupirira Mlengi n’kumene kuli komveka kwambiri.

“Selo Limachita Kuonekeratu Kuti Linachita Kupangidwa”

PAULA KINCHELOE

MBIRI YANGA: Kwa zaka zingapo ndakhala ndikugwira ntchito monga wasayansi wofufuza za maselo ndi tinthu ting’onoting’ono tokhala m’kati mwa maselo a zinthu zamoyo. Panopa ndikugwira ntchito pa yunivesite ya Emory, mu mzinda wa Atlanta, ku Georgia, m’dziko la United States. Ndimagwiranso ntchito yongodzipereka yophunzitsa Baibulo anthu olankhula Chirasha.

Monga mbali ya maphunziro anga, ndinatha zaka zinayi ndikungophunzira za maselo ndi mbali zake zosiyanasiyana. N’taphunzira kwambiri za malangizo okhudzana ndi chibadwa cha munthu amene amakhala m’maselo, tinthu totumiza mauthenga, mapuloteni, ndi zinthu zina zimene zimachitika m’kati mwa maselo, m’pamenenso ndinachita chidwi kwambiri ndi kupangidwa kwake kwaluso, dongosolo lake, ndi kusalakwitsa kwake pochita zinthu. Ndipo ngakhale kuti ndinachita chidwi ndi kuchuluka kwa zinthu zimene anthu aphunzira zokhudza maselo, ndinachita chidwi koposa ndi kuchuluka kwa zinthu zimene sitinazidziwebe. Chifukwa chimodzi chimene chimandichititsa kukhulupirira Mulungu n’choti selo limachita kuonekeratu kuti linachita kupangidwa ndi winawake.

Chifukwa chophunzira Baibulo ndadziwa kuti Yehova Mulungu ndiye Mlengi. Ndikukhulupirira kuti Mulungu si kuti ali chabe wopanga zinthu wanzeru komanso ndi Atate wachifundo ndi wachikondi amene amandidera nkhawa. Baibulo limafotokoza cholinga cha moyo ndipo limapereka chiyembekezo cha tsogolo losangalatsa.

Achinyamata amene akuphunzitsidwa chisinthiko kusukulu mwina sangadziwe kuti akhulupirire chiyani. Nthawi imeneyi ikhoza kukhala yosokoneza kwa iwo. Ngati amakhulupirira Mulungu, chimenechi chimakhala chiyeso cha chikhulupiriro chawo. Koma akhoza kuthana ndi chiyeso chimenechi mwa kuona zinthu zamoyo zochititsa chidwi zomwe zili paliponse ndi kupitiriza kumudziwa bwino kwambiri Mlengi ndi makhalidwe ake. Ineyo ndachita zimenezi ndipo ndazindikira kuti nkhani ya m’Baibulo yonena za kulengedwa kwa zinthu ndi yolondola ndipo sitsutsana ndi sayansi yeniyeni.

“Malamulo Osavuta Kumva”

ENRIQUE HERNÁNDEZ-LEMUS

MBIRI YANGA: Ndine mtumiki wa nthawi zonse wa Mboni za Yehova. Ndinenso katswiri wa sayansi ya malamulo amene zinthu zimayendera ndipo ndikugwira ntchito pa National University of Mexico. Ntchito imene ndikugwira panopa ndi yofufuza mmene nyenyezi zimapangikira ndi momwe zimatenthera. Ndagwiraponso ntchito yokhudzana ndi malangizo ovuta kumvetsa amene amakhala m’maselo, okhudza chibadwa cha zamoyo.

Moyo ndi wapamwamba kwambiri moti sukanatheka kungopangika mwangozi. Mwachitsanzo, taganizirani kuchuluka kwa malangizo okhudza chibadwa amene amakhala m’kati mwa selo. Kuti kanthu kakang’ono kamodzi kamene kamakhala m’kati mwa selo kapangike kokha, zingatheke ulendo umodzi wokha pa maulendo 9 thililiyoni alionse, kutanthauza kuti tingangoti zimenezi n’zosatheka. Ndikuganiza kuti n’kupanda nzeru kukhulupirira kuti mphamvu zopanda winawake wozitsogolera zikanatha kupanga zokha, osati kokha kanthu kakang’ono kamodzi kokhala m’kati mwa selo, koma zinthu zonse zopangidwa mwaluso zomwe zili m’kati mwa zinthu zamoyo.

Chinanso, ndikaona khalidwe lodabwitsa la zinthu zosiyanasiyana, kuyambira pa tinthu ting’onoting’ono tosaoneka ndi maso mpaka pa kayendedwe ka zinthu zakuthambo, ndimagoma ndi malamulo osavuta kumva amene zinthu zimenezi zimayendera. Kwa ine, malamulo amenewa amasonyeza zambiri kuposa pa kungosonyeza kuti anapangidwa ndi katswiri wa masamu. Amakhala ngati siginecha ya katswiri wa zojambulajambula waluso kwambiri.

Anthu nthawi zambiri amadabwa ndikawauza kuti ndine wa Mboni za Yehova. Nthawi zina amandifunsa kuti ndimatha bwanji kukhulupirira kuti Mulungu alipo. M’pomveka kuti anthuwa amadabwa choncho, chifukwa zipembedzo zambiri sizilimbikitsa anthu awo kufunsa kuti aone umboni wa zimene aphunzitsidwa kapena kuti afufuze zikhulupiriro zawo. Komabe, Baibulo limatilimbikitsa kugwiritsa ntchito mphamvu zathu za “kulingalira.” (Miyambo 3:21) Umboni wonse wosonyeza kuti zinthu zamoyo zinapangidwa ndi winawake wanzeru, limodzi ndi umboni wochokera m’Baibulo, umanditsimikizira osati kokha kuti Mulungu alipo, komanso kuti amamva mapemphero athu.

[Mawu a M’munsi]

^ ndime 3 Maganizo a akatswiri amene alembedwa mu nkhani ino sikuti akuimira maganizo a owalemba ntchito.

[Mawu a Chithunzi patsamba 22]

Mars in background: Courtesy USGS Astrogeology Research Program, http://astrogeology.usgs.gov