Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Kodi Ndili Ndi Matenda Ovutika Kudya?

Kodi Ndili Ndi Matenda Ovutika Kudya?

Zimene Achinyamata Amadzifunsa

Kodi Ndili Ndi Matenda Ovutika Kudya?

“Nthawi zina ndikakhala pansi kuti ndidye, ndimachita mantha n’kuyamba kunjenjemera. Ndimaopa kuti ndinenepa. Ndimadziuza kuti, ‘Ndiyenera kuonda ndi makilogalamu ena awiri.’”—Anatero Melissa. *

“Ndimafuna kukhala wokongola, ndipo ndimaopa kwambiri kunenepa. Koma sindikufuna kuti aliyense adziwe kuti ndimasanza dala ndikatha kudya. N’zochititsa manyazi kwambiri.”—Anatero Amber.

“Ndimadziuza kuti, ‘ . . . Lero ndichita bwino . . . ’ Kenaka panthawi inayake tsiku likamapita, ndimadya zakudya zambiri zedi. Ndimadziimba mlandu, ndipo ndimangofuna kufa.”—Anatero Jennifer.

MUMAFUNA kuti muzioneka bwino, ndipo palibe cholakwika ndi zimenezo. Mumafuna kutonthozedwa mukakhala ndi nkhawa kapena mukamavutika maganizo. Palibenso cholakwika chilichonse ndi zimenezo. Koma ngati muli ngati atsikana amene tawatchula pano, mwina muli ndi vuto. Ngati ndi choncho, simuli nokha. Zoona zake n’zoti achinyamata mamiliyoni ambiri, makamaka atsikana, ali ndi matenda ovutika kudya.

Tiyeni tione bwinobwino matenda a anorexia, bulimia, ndi a kudya kwambiri. Alionse mwa matenda amenewa ali ndi zizindikiro zake zapadera, koma onsewa amakhudzana ndi kuona zakudya molakwika. Ngati mukuona kuti zimene mumachita zikufanana ndi zilizonse zomwe zafotokozedwa pansipa, dziwani kuti thandizo lilipo. Mukhoza kuchira!

Matendawa Mwachidule

ANOREXIA. Kaya akhale woonda bwanji, mtsikana wodwala anorexia akadziyang’ana pa galasi, amaona kuti ndi wonenepa. Kuti aonde, amachita zinthu zonyanyira kwambiri. Mtsikana wina wodwala matendawa anati: “Ndinkangokhalira kuwerengetsera kuchuluka kwa chakudya chomwe ndinkadya. Ndinkasankhiratu mosamala chakudya chomwe ndidye mlungu umenewo, ndipo ndinkadzimana chakudya ndi kuchita kwambiri masewera olimbitsa thupi ndikaganiza kuti ndadya kwambiri. Ndinafika pomamwa mapilisi sikisi pa tsiku otsegulitsa m’mimba.”

Pasanapite nthawi yaitali, zizindikiro za matenda a anorexia zimayamba kuoneka. Kuonda ndi chizindikiro chofala, koma wodwalayo akhozanso kuthothoka tsitsi, kukhala ndi khungu lokhakhala, kutopa, ndi kukhala ndi mafupa osalimba. Akhoza kumadumphitsa miyezi ina osasamba kapenanso kusiyiratu kusamba kwa miyezi ingapo yotsatizana.

Mwina zizindikiro zimenezi zikuoneka ngati zosaopsa, koma dziwani izi: Matenda a “anorexia” akhoza kupha munthu. Pa kafukufuku wina anapeza kuti m’kupita kwa nthawi, anthu okwana 10 pa anthu 100 alionse odwala matendawa amafa chifukwa cha matenda awowo, nthawi zambiri chifukwa choti ziwalo zawo zina zam’kati zimasiya kugwira ntchito kapena chifukwa cha mavuto ena okhudzana ndi kusadya bwino.

BULIMIA. M’malo mopewa zakudya, mtsikana wodwala bulimia amatha kudya pa maola awiri okha zakudya zimene munthu wabwinobwino akhoza kudya kwa mlungu wathunthu kapena kuposa pamenepo. Akatero amachotsa m’mimba mwake zinthu zomwe wadyazo, nthawi zambiri mwa kudzisanzitsa kapena kumwa mankhwala otsegulitsa m’mimba kapena okodzetsa.

Kudya kwambiri nthawi zambiri kumachitika mwakabisira. Mtsikana wina anati: “Ndikaweruka kusukulu n’kufika kunyumba anthu ena asanafike, ndinkakonda kudya kwambiri. Ndinkayesetsa kubisa chilichonse chomwe chikanandigwiritsa.” Koma akatha kudya kwambiri, ankayamba kudziimba mlandu. Iye anati: “Ndinkaipidwa kwambiri, koma ndinkadziwa kuti pali njira yofafanizira zochita zangazo. Ndinkapita m’chipinda chapamwamba n’kukasanza. Ndikatero ndinkamva bwino komanso ndinkaona kuti zinthu zikundiyendera.”

Koma kuchotsa zakudya m’mimba n’koopsa, ngakhale kuzioneka ngati kuli ndi phindu. Kumwa kwambiri mankhwala otsegulitsa m’mimba kumafooketsa matumbo ndipo kungawachititse kutupa kapena kuyamba matenda. Kusanza pafupipafupi kukhoza kutha madzi m’thupi, kuwoletsa mano, kuwononga kholingo, ngakhalenso kusiyitsa mtima kugwira bwino ntchito.

MATENDA ODYA KWAMBIRI. Mofanana ndi munthu wodwala bulimia, munthu amene akudwala matenda odya kwambiri amadya chakudya chochuluka zedi. Koma kusiyana kwake n’koti iye sachotsa chakudyacho m’mimba. Chifukwa cha zimenezi, munthu wodya kwambiri akhoza kukhala wonenepa kwambiri. Koma ena akatha kudya kwambiri amadzimana chakudya kapena amachita kwambiri masewera olimbitsa thupi. Nthawi zina, anthu akamachita zimenezi n’kumakhalabe oonda, achibale awo kapena anzawo sadziwa zoti munthuyo ali ndi vuto lodya kwambiri.

Mofanana ndi anthu odwala anorexia kapena bulimia, anthu odya kwambiri amaona zakudya molakwika. Mtsikana wina, ponena za iyeyo ndi anthu ena odwala matenda amenewa, anati: “Chakudya ndi mnzathu wapamtima wachinsinsi, ndipo mwina ndicho mnzathu yekhayo amene tili naye.” Wina anati: “Tikamadya, palibenso china chilichonse chomwe timaganizira. Chakudya chimasanduka chinthu chofunika kwambiri kuposa zonse ndipo chimatichititsa kumva bwino. Kenaka tikatha kudyako, timadziimba mlandu ndipo timavutika maganizo.”

Ngakhale popanda kusanza kapena kutsegula m’mimba, kudya kwambiri n’koopsa. Kungayambitse matenda a shuga, othamanga magazi, a mtima, ndi matenda ena ambiri. Kungamusokonezenso munthu maganizo kwambiri.

Kodi Zingakuchitikireni Inuyo?

N’zoona kuti anthu ambiri amene akufuna kuonda kapena amene akufuna kumachita zinthu zolimbitsa thupi si ndiye kuti ali ndi matenda ovutika kudya. Komabe, pambuyo powerenga zomwe zili mu nkhani ino, mungaone ngati mukuchita zinthu zimene zingayambitse matenda amenewa. Dzifunseni kuti:

▪ Kodi ndimachita manyazi ndi zizolowezi zanga zokhudza chakudya kapena kadyedwe kanga kachilendo?

▪ Kodi ndimabisira anthu ena zizolowezi zanga za kadyedwe?

▪ Kodi chakudya chakhala chinthu chofunika kwambiri pamoyo wanga?

▪ Kodi ndimakwera sikelo koposa kamodzi patsiku?

▪ Kodi ndine wokonzeka kuchita chilichonse kuti ndionde?

▪ Kodi ndayeserapo kudzisanzitsa, kumwa mankhwala otsegulitsa m’mimba, kapena okodzetsa?

▪ Kodi kadyedwe kanga kakusokoneza kachezedwe kanga ndi anthu ena? Mwachitsanzo, kodi ndimakonda kukhala ndekha m’malo mokhala ndi anthu ena, kuti ndithe kudya kwambiri kapena kusanza kapenanso kutsegula m’mimba mwakabisira?

Ngati mayankho anu ku mafunso amenewa akusonyeza kuti muli ndi vuto, dzifunseni kuti:

▪ Kodi ndinedi wosangalala kumakhala chonchi?

Koma kodi mungatani?

Chitanipo Kanthu Panopa!

Chinthu choyamba kuchita ndicho kuvomereza kuti muli ndi vuto. Danielle anati: “Nditaganizira nkhaniyi mwachifatse, ndinazindikira kuti maganizo anga ndi zochita zanga zinali zofanana ndi za atsikana odwala matenda a anorexia. Zinali zoopsa kuzindikira kuti ndinkachita zinthu zofanana ndi zimene iwowo ankachita.”

Kenaka, pempherani kwa Yehova za vuto lanulo. * M’pempheni kuti akuthandizeni kuzindikira chomwe chikuyambitsa matenda anuwo kuti muthe kuwagonjetsa. Mungapemphere ngati mmene anapempherera Davide, kuti: “Mundisanthule, Mulungu, nimudziwe mtima wanga; mundiyese nimudziwe zolingalira zanga. Ndipo mupenye ngati ndili nawo mayendedwe oipa, nimunditsogolere pa njira yosatha.”—Salmo 139:23, 24.

Koma mwina mukhoza kuona kuti simukufuna kusiyana ndi matenda anuwo. Mwina mukhoza kukhala mutayamba kudalira matendawo, ngati mmene amachitira munthu amene wakodwa mu msampha wochita zinthu zinazake zoipa. Imeneyinso ndi nkhani imene mukhoza kumuuza Yehova m’pemphero. Zimenezi n’zimene Danielle anafunika kuchita. Iye akuvomereza kuti, “Poyamba, sindinkafuna kuchira. Choncho ndinafunika kupemphera kuti ndikhale ndi mtima wofuna kuchira.”

Chachitatu, lankhulani ndi kholo lanu kapena wachikulire wina amene angathe kukuthandizani. Achikulire amene akukufunirani zabwino sangakuchititseni manyazi. M’malo mwake, adzayesetsa kutsanzira Yehova, amene ponena za iye Baibulo limati: “Sanapeputsa ndipo sananyansidwa ndi zunzo la wozunzika; ndipo sanam’bisira nkhope yake; koma pom’fuulira Iye, anamva.”—Salmo 22:24.

N’zoona kuti sizophweka kuti munthu afike pochira. Nthawi zina pangafunike kupeza thandizo kwa akatswiri odziwa za matenda amenewa. * Chinthu chofunika ndicho kuchitapo kanthu. Zimenezo n’zimene mtsikana wina wodwala bulimia anachita. Iye anati: “Tsiku lina, ndinayamba kuzindikira kuti kusanza ndi kutsegula m’mimba kukundilamulira. Komabe, sindinadziwe ngati ndingathe kusiya. Pomalizira pake, ndinachita chinthu chovuta kwambiri kuposa zonse zomwe ndachitapo. Ndinapempha thandizo.”

Inunso mukhoza kuchita zomwezo!

Nkhani zina zakuti “Zimene Achinyamata Amafunsa,“ mungazipeze pa adiresi yathu ya pa Intaneti ya www.pr418.com.

[Mawu a M’munsi]

^ ndime 3 Tasintha mayina ena mu nkhani ino.

^ ndime 32 Mukavutika maganizo, mukhoza kukhala otsimikiza kuti Yehova amakusamalirani mwa kusinkhasinkha za malemba ngati otsatirawa: Eksodo 3:7; Salmo 9:9; 34:18; 51:17; 55:22; Yesaya 57:15; 2 Akorinto 4:7; Afilipi 4:6, 7; 1 Petro 5:7; 1 Yohane 5:14.

^ ndime 35 Akristu ayenera kuonetsetsa kuti thandizo lililonse lomwe akufuna kutsatira silikusemphana ndi mfundo za m’Baibulo.

ZOTI MUGANIZIRE

▪ Kodi mukuganiza kuti mwina muli ndi matenda ovutika kudya? Ngati ndi choncho, kodi mungapite kwa ndani kuti akuthandizeni?

▪ Kodi mungathandize bwanji mnzanu amene ali ndi matenda ovutika kudya?

[Bokosi patsamba 19]

“Ndikuganiza kuti muli ndi vuto . . .”

Ngati wachibale wanu kapena mnzanu wanena mawu amenewo, pewani kudziikira kumbuyo. Tiyerekeze kuti mnzanu waona kuti msoko wa kumbuyo kwa diresi lanu ukuphwethuka. Kodi simungamuthokoze chifukwa chokudziwitsani zimenezi msokowo usanaphwethukiretu? Baibulo limati: “Lilipo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.” (Miyambo 18:24) Munthu wina akakuuzani nkhawa imene ali nayo chifukwa choti akuganiza kuti muli ndi vuto linalake, ndiye kuti ameneyu akuchita zinthu ngati bwenzi loterolo!

[Bokosi/Chithunzi patsamba 19]

“Ndinkafuna kuonda”

“Ndinayamba kuonda. Kenaka anandichotsa mano akuluakulu, choncho ndinkalephera kudya. Zimenezi n’zimene zinandiyambitsa matenda a anorexia. Ndinayamba kuda nkhawa monyanyira ndi kaonekedwe kanga. Kaya ndionde bwanji, ndinkaona kuti sindinafikepo. Kulemera kumene ndinafika n’taonda kwambiri kunali kochititsa mantha. Ndinawononga kwambiri thupi langa. Panopa zikhadabo zanga sizikula. Ndinasokoneza mphamvu ya thupi langa yodziwa nthawi. Ndapita pachabe kanayi. Ndinasiya kusamba nthawi yanga isanakwane, ndipo thupi langa siligwira ntchito bwino. Ndilinso ndi matenda a m’matumbo. Zonsezi zinandichitikira chifukwa ndinkafuna kuonda.”—Anatero Nicole.

[Bokosi patsamba 20]

Mukayambiranso

Mwina mukhoza kuthana ndi matenda anu ovutika kudya, kenaka n’kuyambiranso kudwala patatha milungu kapena miyezi ingapo. Zimenezi zikachitika, musataye mtima. Baibulo limavomereza kuti “wolungama amagwa kasanu ndi kawiri.” (Miyambo 24:16) Vutoli likayambiranso, sindiye kuti mwalephera. Zikungogogomezera kufunika kokhala wotsimikiza mtima, kozindikira zizindikiro zokusonyezani kuti mwatsala pang’ono kuyambiranso, ndi kuti mwina mukufunika kulankhulanso ndi anthu okufunirani zabwino amene angathe kukuthandizani.

[Bokosi/Chithunzi patsamba 20]

Werengani zina zokhudza matendawa

Ngati mukudwala matenda ovutika kudya, mungachite bwino kuwerenga zambiri za matendawa. Ngati mukudziwa zambiri zokhudza vuto limeneli, zimakhala zosavutirapo kuthana nalo. N’zachidziwikire kuti mungapindule mutawerenga mfundo zothandiza zomwe zinatuluka mu Galamukani! ya February 8, 1999, masamba 23 mpaka 32, ndi ya May 8, masamba 13 mpaka 15.

[Bokosi patsamba 21]

MALANGIZO KWA MAKOLO

Ngati mwana wanu wamkazi akudwala matenda ovutika kudya, kodi mungatani? Choyamba, werengani mosamala mfundo zimene zili mu nkhani ino ndi mu nkhani zina zimene zatchulidwa pa tsamba 20. Yesetsani kumvetsa chifukwa chimene wayambira kuchita zinthu zimenezi.

Zaonedwapo kuti anthu ambiri odwala matenda ovutika kudya amadziona kuti ndi opanda pake ndipo amafuna kuchita bwino kwambiri zinthu, choncho amadziikira zolinga zoti sangathe kuzikwanitsa. Onetsetsani kuti si inuyo amene mukumulimbikitsa kukhala ndi makhalidwe amenewa. Muzimulimbikitsa mwana wanu wamkazi. (Yesaya 50:4) Ndipo kuti muthetse mtima wodziikira zolinga zosatheka kukwanitsa, “kulolera [kwa inuyo] kudziwike kwa anthu onse.”—Afilipi 4:5, NW.

Chinanso, onani bwinobwino mmene mumaonera nkhani ya chakudya ndi kunenepa kapena kuonda. Kodi mwina mosadziwa mumagogomezera kwambiri nkhani zimenezi, kaya mwa zonena zanu kapena chitsanzo chanu? Kumbukirani kuti achinyamata amada nkhawa kwambiri ndi kaonekedwe kawo. Ngakhale kunyogodola za kunenepa kwa paubwana kapena kukula kwambiri kwa paunyamata kukhoza kupatsa wachinyamata maganizo oipa, popeza achinyamata sachedwa kukhulupirira zinthu. Zimenezi zikhoza kudzamubweretsera mavuto m’tsogolo.

Mukaganizira mozama za nkhaniyi n’kuipempherera, kambiranani momasuka ndi mwana wanu wamkazi.

▪ Konzekerani mosamala zomwe mudzanene ndi nthawi yomwe mudzazinenere.

▪ Nenani momveka bwino nkhawa yanu ndi cholinga chanu chofuna kumuthandiza.

▪ Musadabwe ngati poyamba akudziikira kumbuyo.

▪ Mvetserani moleza mtima.

Chofunika kwambiri, muzimuthandiza mwana wanu wamkaziyo pamene akuyesetsa kuti achire. Banja lonselo lizichitira limodzi zinthu zomuthandiza kuti achire!

[Chithunzi patsamba 21]

Mungafunike kupemphera kuti mukhale ndi mtima wofuna kuchira