Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

KODI ZINACHITIKIRA KUTI?

1. Kodi Mgonero wa Ambuye unachitikira kuti koyamba?

Lembani mzere mozungulira yankho lanu pa mapupa.

Nazarete

Yeriko

Yerusalemu

Betelehemu

◆ Kodi buledi wopanda chofufumitsa amaimira chiyani?

․․․․․

◆ Kodi vinyo wofiira amaimira chiyani?

․․․․․

Kambiranani: Kodi Mgonero wa Ambuye umatikumbutsa chiyani? N’chiyani chimene chimakusangalatsani pa mwambo umenewu?

ZINACHITIKA LITI?

Tchulani anthu amene analemba mabuku a m’Baibulo amene ali m’munsiwa, ndipo lembani mzere wolumikiza buku ndi nthawi imene anamaliza kulilemba.

1077 B.C.E. 1040 B.C.E. 580 B.C.E 55 C.E 66 C.E

2. 2 Samueli

3. 2 Mafumu

4. 2 Akorinto

NDINE NDANI?

5. Anzanga anandibweretsera madzi kuti ndimwe, koma ndinawathira pansi ngati magazi.

NDINE NDANI?

6. Ena anati iwowo ndi anthu anga; ena anati iwowo ndi anthu a Paulo, a Apolo, kapena a Khristu.

KUCHOKERA M’MAGAZINI INO

Yankhani mafunso awa, ndipo tchulani mavesi a m’Baibulo omwe akusowa.

Tsamba 8 Kodi timafunikira kutsimikizira chiyani? (Afilipi 1:․․․)

Tsamba 9 Kodi mungakhale bwanji anzeru? (Miyambo 13:․․․)

Tsamba 20 Kodi ndani amene adzakhale wamkulu mu “ufumu wa kumwamba”? (Mateyo 18:․․․)

Tsamba 29 Kodi ndi ndani amene sadzalowa mu Ufumuwo? (Aefeso 5:․․․)

Zithunzi Zoti Ana Apeze

Kodi mungapeze zithunzi izi m’magazini ino? Fotokozani nokha zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.

(Mayankho ali patsamba 19)

MAYANKHO A MAFUNSO A PA TSAMBA 31

1.Yerusalemu—Mateyo 21:10, 17, 18; 26:17-19.

◆ Thupi la Yesu.—Mateyo 26:26.

◆ Magazi a Yesu.—Mateyo 26:27, 28.

2. Gadi, Natani, 1040 B.C.E

3. Yeremiya, 580 B.C.E.

4. Paulo, 55 C.E.

5. Davide.—2 Samueli 23:15-17.

6. Kefa, kapena Petulo.—Yohane 1:42; 1 Akorinto 1:12.