Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi chithunzichi chalakwika pati?

Tchulani zinthu zitatu pa chithunzichi zomwe sizikugwirizana ndi nkhani ya m’Baibulo ya pa Yohane 13:2-14.

1. ․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․

2. ․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․

3. ․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi m’nkhaniyi Yesu anasonyeza makhalidwe otani? Kodi mungamutsanzire bwanji pochita zinthu ndi anthu a m’banja mwanu?

Kuchokera M’magazini Ino

Yankhani mafunsowa, ndipo lembani vesi kapena mavesi a m’Baibulo omwe akusowapo.

TSAMBA 5 Tchulani chifukwa chimodzi chimene chimachititsa kuti anthu ena ‘atsimikize mitima yawo kuchita zoipa?’ Mlaliki 8:․․․

TSAMBA 8 Kodi anthu oipa ali ndi tsogolo lotani? Salmo 73:․․․

TSAMBA 10 Kodi Mulungu amawaika kutali motani machimo athu? Salmo 103:․․․

TSAMBA 27 Kodi Yesu anachita chiyani chimene chingalimbikitse achinyamata ndiponso anthu ena amene ali ndi mavuto enaake m’thupi? Mateyo 4:․․․

Zithunzi Zoti Ana Apeze

Kodi mungapeze zithunzi izi m’magazini ino? Fotokozani zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.

Ndani Amene Ali Mbali ya Mzera wa Banja la Yesu?

Onani zokuthandizani kupeza yankho. Onaninso malembawo. Kenaka lembani mayina olondola pa mizereyi.

4. ․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․

ZOKUTHANDIZANI: ‘Ndinasamutsidwa kuti ndisaone imfa.’

Werengani Aheberi 11:5.

5. ․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․

ZOKUTHANDIZANI: Ndinakhala ndi moyo wautali kuposa munthu aliyense wotchulidwa m’Baibulo.

Werengani Genesis 5:27.

6. ․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․

ZOKUTHANDIZANI: Mwana wanga anamanga chingalawa.

Werengani Genesis 5:28, 29 ndi Aheberi 11:7.

▪ Mayankho ali pa tsamba 22

MAYANKHO A MAFUNSO A PA TSAMBA 31

1. Yesu anasambitsa mapazi, osati manja a ophunzira ake.

2. Palibe ophunzira aliyense amene anam’thandiza Yesu pantchitoyi.

3. Komanso Yesu anapukuta mapazi a ophunzirawo.

4. Inoke.—Luka 3:37.

5. Metusela.—Luka 3:37.

6. Lameki.—Luka 3:36.

[Mawu a Chithunzi patsamba 31]

Third circle: Northern Territory Archives Service, Joe DAVIS, NTRS 573