Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Zinachitikira Kuti?

1. Yesu anaperekedwa ali kuti?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Mateyo 26:36- 56.

Pa mapu awa lembani mzere wozungulira yankho lanu.

Munda wa Getsemane

Kachisi

Nyumba ya bwanamkubwa

Dziwe la Siloamu

▪ Kodi ndi wophunzira uti amene anapereka Yesu?

․․․․․

▪ Kodi ndi wophunzira uti amene anadula khutu la kapolo wa mkulu wa ansembe?

․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi Yesu anachita chiyani wotsatira wake atagwiritsa ntchito chida kuti amuteteze? Nanga mukuphunzirapo chiyani pa zimene anauza ophunzira ake?

Kuchokera M’magazini Ino

Yankhani mafunsowa, ndipo lembani vesi kapena mavesi a m’Baibulo omwe akusowa

TSAMBA 3 Kodi Yesu ananena kuti anabadwira kudzatani? Yohane 18:․․․

TSAMBA 5 NDI 6 Kodi Paulo anati tizikhala ogwirizana mu chiyani? 1 Akorinto  1:․․․

TSAMBA 11 Chimachitika n’chiyani anthu akadziwa zoona zake za zikhulupiriro za makolo? Yohane 8:․․․

TSAMBA 20 Kodi zonena zanu zimasonyeza chiyani? Luka 6:․․․

Zithunzi Zoti Ana Apeze

Kodi mungapeze zithunzi izi m’magazini ino? Fotokozani zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.

Ndani Ali mu Mzere wa Banja la Yesu?

Onani zokuthandizani kupeza yankho. Onaninso malembawo. Kenaka lembani mayina olondola pa mizereyi.

2. ․․․․․

ZOKUTHANDIZANI: Ndinkadziwika monga “mlaliki wa chilungamo.”

Werengani 2 Petulo 2:5.

3. ․․․․․

ZOKUTHANDIZANI: Ndine mwana wa Nowa amene nthawi zonse ndimakhala woyamba kutchulidwa.

Werengani Genesis 6:10.

4. ․․․․․

ZOKUTHANDIZANI: M’nthawi yanga “dziko lapansi linagawikana.”

Werengani Genesis 10:25.

▪ Mayankho ali pa tsamba 30

MAYANKHO A MAFUNSO A PA TSAMBA 31

1. Munda wa Getsemane.

▪ Yuda.

▪ Petulo.

2. Nowa.—Luka 3:36.

3. Semu.—Luka 3:36.

4. Pelegi.—Luka 3:35.