Kodi Mungayankhe Bwanji?
Kodi Mungayankhe Bwanji?
Kodi pa Chithunzichi Pakusowa Chiyani?
Werengani Chivumbulutso 12:3. Tsopano yang’anani pa chithunzicho. Kodi ndi zinthu ziti zimene zikusowapo? Lembani mayankho anu m’mizere ili m’munsiyi, ndipo malizitsani kujambula zinthu zimene zikusowazo.
1. ․․․․․
2. ․․․․․
3. ․․․․․
KAMBIRANANI:
Kodi chinjoka chimenechi chikuimira ndani? Kodi iye akuchita chiyani ndi dziko lonse lapansi kumene kuli anthu?
ZOKUTHANDIZANI: Werengani Chivumbulutso 12:9.
Kuchokera M’magazini Ino
Yankhani mafunsowa, ndipo lembani vesi kapena mavesi a m’Baibulo omwe akusowa.
TSAMBA 3 Kodi Mulungu waika chiyani m’maganizo ndi m’mitima ya anthu? Mlaliki 3:․․․
TSAMBA 5 Kodi Mulungu amapereka mphatso yotani? Aroma 6:․․․
TSAMBA 21 Kodi ndi mayina aulemu komanso achipembedzo otani amene Yesu ananena kuti tisamagwiritse ntchito? Mateyo 23:․․․
TSAMBA 27 Kodi munthu wochenjera amatani? Miyambo 22:․․․
Zithunzi Zoti Ana Apeze
Kodi mungathe kupeza zithunzi izi m’magazini ino? Fotokozani zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.
Ndani Ali M’gulu la Makolo a Yesu?
Onani zokuthandizani kupeza yankho. Onaninso malembawo. Kenaka lembani mayina olondola pa mizereyi.
4. ․․․․․
ZOKUTHANDIZANI: Zera Mkusi pamodzi ndi amuna 1 miliyoni anandiukira koma Yehova anawakantha pamaso panga.
Werengani 2 Mbiri 14:9-12.
5. ․․․․․
ZOKUTHANDIZANI: Ndinakonza zakuti Chilamulo cha Yehova chiphunzitsidwe m’midzi ya Yuda.
Werengani 2 Mbiri 17:1, 7-9.
6. ․․․․․
ZOKUTHANDIZANI: Ndinaikidwa m’manda a m’Mudzi wa Davide koma osati m’manda a mafumu.
Werengani 2 Mbiri 21:16-20.
▪ Mayankho ali pa tsamba 13
MAYANKHO A MAFUNSO A PA TSAMBA 31
1. Mutu umodzi ndi khosi limodzi.
2. Nyanga 10.
3. Zisoti zachifumu 7.
4. Asa.—Mateyo 1:7.
5. Yehosafati.—Mateyo 1:8. 6.
6. Yehoramu.—Mateyo 1:8.