Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Zinachitikira Kuti?

1. Kodi Paulo anakumana ndi Timoteyo m’tauni iti?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Machitidwe 16:1-3.

Pamapu awa lembani mzere wozungulira yankho lanu.

Lusitara

Ikoniyo

Derbe

▪ Kodi bambo ake a Timoteyo anali a mtundu wanji? Nanga mayi ake?

․․․․․

▪ Kodi mayi ake a Timoteyo dzina lawo linali ndani?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani 2 Timoteyo 1:5.

․․․․․

▪ Kodi mayi ake a Timoteyo anamuphunzitsa chiyani, nanga n’chifukwa chiyani?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani 2 Timoteyo 3:15.

․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi mungatani kuti mukhale ngati Timoteyo?

Kuchokera M’magazini Ino

Yankhani mafunsowa, ndipo lembani vesi kapena mavesi a m’Baibulo omwe akusowa.

TSAMBA 5 Kodi mungachite chiyani ndi ndalama zanu zina? 1 Akorinto 16:․․․

TSAMBA 5 Kodi mukabwereka ndalama kwa winawake, mumakhala ndani wake? Miyambo 22:․․․

TSAMBA 11 Kodi mfumu Yosiya inatani kuti ithetse kulambira mafano ku Yuda? 2 Mbiri 34:․․․

TSAMBA 19 Kodi n’chifukwa chiyani simuyenera kumangocheza ndi aliyense? Salmo 26:․․․

Zithunzi Zoti Ana Apeze

Pezani zithunzi izi m’magazini ino? Fotokozani m’mawu anuanu zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.

Kodi Mukudziwa Chiyani Chokhudza Aneneri?

Werengani buku la Yona ndipo yankhani mafunso otsatirawa.

2. ․․․․․

Kodi Mulungu anamutuma Yona ku mzinda uti?

3. ․․․․․

Kodi anatumidwa kukapereka uthenga wotani kwa anthu a mumzindawo? Ndipo kodi anthuwo anaulandira bwanji uthengawo?

KAMBIRANANI:

N’chifukwa chiyani Yona anakwiya? Kodi zinali zomveka kuti akwiyedi? N’chifukwa chiyani mwayankha choncho?

▪ Mayankho ali pa tsamba 28

Mayankho a Mafunso a pa Tsamba 31

1. M’tauni ya Lusitara ku Asia Minor.

▪ Bambo ake anali m’Giriki. Mayi ake anali Myuda.

▪ Yunike.

▪ “Malemba opatulika,” omwe ndi Malemba Achiheberi, chifukwa ankafuna kuti iye azilambira Mulungu woona, Yehova.

2. Nineve.—Yona 1:1, 2.

3. Mulungu akufuna kuweruza mzindawo. Anthu ndiponso mfumu yawo analapa.—Yona 1:2; 3:2-9.