Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi N’chiyani Chikusowa Pachithunzichi?

Werengani Numeri 22:21-27. Ndiyeno onani chithunzicho. Lembani mayankho anu m’mizere ili munsiyi, ndipo malizitsani kujambula chithunzicho.

1. ․․․․․

2. ․․․․․

3. ․․․․․

KAMBIRANANI:

N’chifukwa chiyani Balamu anakwiya? Mukaganizira zimene Balamu anachitira bulu wake, kodi mukuona kuti iye anachita bwino, ndipo n’chifukwa chiyani mukuyankha choncho?

Kuchokera M’magazini Ino

Yankhani mafunso omwe ali m’munsiwa, ndipo lembani vesi kapena mavesi a m’Baibulo omwe akusowapo.

MASAMBA 7-8 Kodi kuopa anthu kuli ndi vuto lotani? Miyambo 29:․․․

TSAMBA 7 Kodi chitsiru chimayenda mu chiyani? Mlaliki 2:․․․

TSAMBA 7 Zoganizira za wakhama zimamuchulukitsira chiyani? Miyambo 21:․․․

TSAMBA 22 Kodi akufa sadziwa chiyani? Mlaliki 9:․․․

Zithunzi Zoti Ana Apeze

Kodi mungathe kupeza zithunzi izi m’magazini ino? Fotokozani zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.

Kodi Mumadziwa Chiyani za Aneneri?

Werengani Yeremiya 38:1-13; 39:15-18. Ndiyeno yankhani mafunso otsatirawa.

4. ․․․․․

Tchulani munthu yemwe anapulumutsa Yeremiya, ndipo n’chifukwa chiyani analolera kuchita zimenezi?

5. ․․․․․

Kodi kenako Yeremiya anamuuza chiyani munthuyo?

KAMBIRANANI:

N’chifukwa chiyani Yeremiya analengezabe uthenga wa Yehova ngakhale kuti zinali zoopsa kuchita zimenezi? Mukamatumikira Yehova ngati mmene Yeremiya anachitira, kodi simuyenera kukayikira kuti iye angakuchitireni chiyani?

▪ Mayankho ali pa tsamba 27

MAYANKHO A MAFUNSO A PATSAMBA 31

1. Bulu.

2. Ndodo ya Balamu.

3. Mngelo wa Yehova.

4. Ebedi-Meleki. Iye anadziwa kuti Yeremiya anali mneneri wa Yehova ndipo sanayenere kufa.

5. Yehova adzateteza Ebedi-Meleki powonongedwa Yerusalemu.