Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Mfundo 4: Muzilemekezana

Mfundo 4: Muzilemekezana

Mfundo 4: Muzilemekezana

“Kulalata ndiponso mawu achipongwe zichotsedwe mwa inu.”—Aefeso 4:31.

Mungachite bwanji? Dziwani kuti palibe banja limene mwamuna ndi mkazi wake sasemphana maganizo. Koma zimenezi zikachitika pamafunika kukambirana bwinobwino popanda kulalatirana, kutukwanizana kapena kulankhulana mawu achipongwe. Aliyense ayenera kuchitira mnzake zimene iyeyo angafune kuti mnzakeyo azimuchitira.—Mateyo 7:12.

Kufunika kwake. Mawu angathe kukhala chida chimene tingavulaze nacho wina. Baibulo limati: “Kukhala m’chipululu kufunika kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wong’ung’udza.” (Miyambo 21:19) Mawu amenewa amagwiranso ntchito kwa mwamuna wolongolola ndi wong’ung’udza. Ndipo Baibulo limalangiza makolo kuti: “Musamakwiyitse ana anu, kuti asakhale opsinjika mtima.” (Akolose 3:21) Ana amene amangokhalira kukalipiridwa, amafika poona kuti palibe chimene angachite kuti asangalatse makolo awo. Ndipo angasiye kuyesetsa kuchita zinthu zabwino.

Yesani izi. Yankhani mafunso otsatirawa kuti mudziwe ngati m’banja lanu mumalemekezana.

Kodi m’banja mwathu tikasemphana maganizo, wina amakwiya n’kutuluka m’nyumba akukalipa?

Ndikamalankhula ndi mwamuna, mkazi, kapena ana anga, kodi ndimagwiritsa ntchito mawu achipongwe monga akuti “chitsiru,” “wopusa,” kapena mawu ena otere?

Kodi ndinakulira m’banja limene anthu ake amalankhulana mwachipongwe?

Chitani izi. Ganizirani chinthu chimodzi kapena ziwiri zimene mungachite kuti muzilankhula mwaulemu. (Mwachitsanzo, wina akalakwitsa muzinena kuti, “Ine ndimakhumudwa kwambiri mukachita zimenezi,” m’malo monena kuti, “Nthawi zonse mumachita zimenezi.”)

Mungachite bwino kuuza mwamuna kapena mkazi wanu zimene mukufuna kuchita. Ndiyeno pakapita miyezi itatu, mufunseni kuti akuuzeni ngati mukuchita bwino.

Ganizirani zinthu zimene zingakuthandizeni kuti musamalankhule mawu onyoza kwa ana anu.

Mungachite bwino kupepesa ana anu ngati nthawi zina mwawalankhula mwaukali kapena mowanyoza.

[Chithunzi patsamba 6]

Monga mmene mafunde amaperesera miyala, mawu achipongwe amawononga banja