Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Zoti Banja Likambirane

Zoti Banja Likambirane

Zoti Banja Likambirane

Kodi Chithunzichi Chalakwika Pati?

Werengani Eksodo 12:1-8, 17-20, 24-27; Maliko 14:22-26 ndi Yohane 13:1, 21-30. Ndiyeno onani chithunzichi, chomwe chikusonyeza Mgonero wa Ambuye. Kodi chalakwika pati? Lembani mayankho anu m’munsimu.

1. ․․․․․

2. ․․․․․

3. ․․․․․

KAMBIRANANI:

N’chifukwa chiyani Yesu anagwiritsa ntchito makeke osafufumitsa ngati chizindikiro cha thupi lake?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani 1 Akorinto 5:6-8; Aheberi 4:14, 15.

KODI MUKUDZIWA CHIYANI CHOKHUDZA MFUMU SOLOMO?

4. Kodi mayi ake a Solomo anali ndani?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani 2 Samueli 12:24.

․․․․․

5. Kodi Davide anabereka ana ena aamuna angati ndi amayi ake a Solomo?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani 2 Samueli 11:26, 27 ndi 1 Mbiri 3:5.

․․․․․

KAMBIRANANI:

N’chifukwa chiyani Solomo anali wanzeru kwambiri?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani 1 Mafumu 3:5-14.

Kodi chofunika n’chiyani kuti munthu akhale wanzeru?

ZITHUNZI ZOTI ANA APEZE

Kodi mungathe kupeza zithunzi izi m’magazini ino? Fotokozani zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse?

KUCHOKERA M’MAGAZINI INO

Yankhani mafunsowa, ndipo lembani vesi kapena mavesi a m’Baibulo omwe akusowapo.

TSAMBA 19 Kodi kulingalira mwakuya nkhani zina patokha ndi umboni wa chiyani? Miyambo 1:․․․

TSAMBA 19 Kodi Yesu analangiza ophunzira ake kuti azitani akafuna kupemphera? Mateyo 6:․․․

TSAMBA 28 Kodi “malemba opatulika” angatithandize kutani? 2 Timoteyo 3:․․․

TSAMBA 29 Kodi “chitonthozo cha m’Malemba” chingatipatse chiyani? Aroma 15:․․․

● Mayankho ali patsamba 14

MAYANKHO A MAFUNSO A PATSAMBA 31

1. Payenera kukhala atumwi 11, osati 12.

2. Makekewo ayenera kukhala opanda zofufumitsa.

3. Inali nyama ya nkhosa, osati ya nkhumba.

4. Bateseba.

5. Davide ndi Bateseba anali ndi ana ena anayi kuwonjezera pa Solomo.