Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Zoti Banja Likambirane

Zoti Banja Likambirane

Zoti Banja Likambirane

Kodi Chithunzichi Chalakwika Pati?

Werengani Genesis 4:1-8. Ndiyeno onani chithunzichi. Kodi chalakwika pati? Lembani mayankho anu m’munsimu.

1. ․․․․․

2. ․․․․․

3. ․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi Kaini anatani Yehova Mulungu atasonyeza kuti wakonda m’bale wake Abele? Ngati makolo anu atasonyeza kuti akukonda kwambiri m’bale wanu, kodi inuyo muyenera kupewa chiyani, ndipo n’chifukwa chiyani?

KODI MUKUDZIWA CHIYANI CHOKHUDZA MTUMWI NATANAYELI?

4. Kodi Natanayeli ayenera kuti ankadziwikanso ndi dzina liti?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Luka 6:14; Yohane 1:44-46.

․․․․․

5. Tchulani khalidwe labwino la Natanayeli limene Yesu anamuyamikira nalo.

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Yohane 1:47.

․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi mungatsanzire bwanji Natanayeli? Kodi kuchita zimenezi kungakuthandizeni bwanji?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Salimo 24:3-5; 34:13-16.

ZITHUNZI ZOTI ANA APEZE

Pezani zithunzi izi m’magazini ino. Fotokozani zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.

KUCHOKERA M’MAGAZINI INO

Yankhani mafunsowa, ndipo lembani vesi kapena mavesi a m’Baibulo omwe akusowapo.

TSAMBA 5 Kodi maganizo a anthu amakhala otani? Genesis 8:․․․

TSAMBA 6 Kodi tiyenera kuchita zinthu zonse motani? Aheberi 13:․․․

TSAMBA 24 Kodi tikamachita zinthu tiyenera kuganizira chiyani? 1 Akorinto 9:․․․

TSAMBA 26 Kodi chingachitike n’chiyani ngati mumayang’ana mphepo kapena mitambo? Mlaliki 11:․․․

● Mayankho ali patsamba 21

MAYANKHO A MAFUNSO A PATSAMBA 31

1. Ndi anthu awiri okha amene anapereka nsembe.

2. Kaini anapereka nsembe ya zipatso.

3. Abele anapereka nsembe ya nkhosa osati ya ng’ombe.

4. Batolomeyo.

5. Analibe chinyengo.