GALAMUKANI! July 2014 | Kodi Mungatani Mutakumana Ndi Vuto Lalikulu?

Kodi mungatani mutakumana ndi vuto linalake lalikulu?

Zochitika Padzikoli

Nkhani zake ndi monga: kudera limene chiwerengero cha akazi omwa mowa mwauchidakwa ndi chokwera kuposa cha amuna, malo amene anapezako zinthu zamoyo komanso dziko limene anthu amalandira ndalama akachepetsa thupi.

NKHANI YAPACHIKUTO

Kodi Mungatani Mutakumana Ndi Vuto Lalikulu?

Baibulo lingakuthandizeni kudziwa zomwe mungachite.

NKHANI YAPACHIKUTO

Katundu Wanu Yense Atawonongeka

Katundu yense wa Kei anawonongeka mu 2011 chifukwa cha tsunami amene anachitika ku Japan. Mabungwe ndi anzake anamuthandiza koma linamuthandiza kwambiri ndi vesi lina la m’Baibulo.

NKHANI YAPACHIKUTO

Atakupezani Ndi Matenda Aakulu

Mabel ankagwira ntchito yothandiza anthu kuchita mafizo. Koma atapangidwa opaleshoni chifukwa cha chotupa cha muubongo, ankafunika kuchita mafizo amene ankachititsa anthu ena odwala omwe ankawasamalira poyamba.

NKHANI YAPACHIKUTO

Munthu wa M’banja Lanu Akamwalira

Zaka 16 zapitazo, anthu 5 a m’banja la Ronaldo anamwalira pa ngozi ya galimoto. Ngakhale kuti imfayi imamupwetekabe, panopa ali ndi mtendere wa mumtima.

MFUNDO ZOTHANDIZA MABANJA

Kodi Mungasonyeze Bwanji Khalidwe Labwino Mukamatumiza ndi Kulandira Mameseji pa Foni?

Kodi mukuona kuti n’kupanda ulemu kusiya kaye kucheza ndi mnzanu kuti muwerenge meseji? Kapena mukuganiza si bwino kumangopitirizabe kucheza ndi mnzanuyo osawerenga kaye meseji imene mwalandira?

ANTHU NDI MAYIKO

Dziko la Ireland

Werengani zokhudza anthu ansangala a ku Emerald Isle.

KUCHEZA NDI ANTHU

Katswiri Wasayansi Akufotokoza za Chikhulupiriro Chake

Mfundo ziwiri zomwe zinathandiza Wenlong He kuti ayambe kukhulupirira zoti kuli Mlengi.

ZIMENE BAIBULO LIMANENA

Zipembedzo

Baibulo limanena chifukwa chake pali zipembedzo zambiri chonchi.

KODI ZINANGOCHITIKA ZOKHA?

Achule Amene Amaswa Modabwitsa Kwambiri

N’chifukwa chiyani anthu ena amene amakhulupirira kuti zamoyo zinachita kusintha kuchokera ku zinthu zina, amanena kuti mfundo yakuti achulewa anachita kusintha mwa pang’onopang’ono ndi yosamveka?

Zina zimene zili pawebusaiti

Kodi Ndingafotokoze Bwanji Zimene Ndimakhulupirira pa Nkhani ya Kugonana?

Ngati mutafunsidwa kuti: ‘Kodi sunagonanepo ndi munthu chibadwire?’ kodi mungathe kugwiritsa ntchito Baibulo poyankha?

Kodi Ndingatani Ngati Anthu Ena Akukonda Kunena za Ine?

Kodi mungatani kuti zinthu zabodza zimene anthu akufalitsa zokhudza inuyo zisawononge mbiri yanu?

Kodi Ndingatani Kuti Ndisamachite Zinthu Mozengereza?

Werengani malangizo amene angakuthandizeni kuti musamachite zinthu mozengereza

Zimene Zinachitika Mose Ali Kamwana

Kodi anthu amene ali pachithunziwo ndi ndani? Werengani nkhani ya m’Baibulo yopezeka pa Ekisodo chaputala 2 kuti muwadziwe.