Mawu Oyamba
Makhalidwe 6 Amene Muyenera Kuphunzitsa Ana Anu
Kodi mumafuna kuti mwana wanu azidzadziwika ngati munthu wotani akadzakula?
Wodziletsa?
Wodzichepetsa?
Wopirira?
Wodalirika?
Woganiza bwino?
Wokhulupirika?
Ana sangakhale ndi makhalidwe amenewa paokha. Amafunika kuti inuyo makolo muwathandize.
Magaziniyi yafotokoza makhalidwe ofunika 6 omwe muyenera kuphunzitsa ana anu kuti adzakhale anthu odalirika.