Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Kodi Dzikoli Latsala Pang’ono Kutha?

Kodi Dzikoli Latsala Pang’ono Kutha?

Ngakhale kuti maulendo angapo anthu akhala akunena tsiku lenileni lomwe dzikoli lidzathe koma zomwe ankaganizazo sizinachitike. Ndiye kodi dzikoli lidzathadi?

KODI BAIBULO LIMANENA ZOTANI?

  • Kodi mapeto a dzikoli adzakhala otani?

  • Kodi dzikoli lidzatha liti?

  • Kodi mudzapulumuka?

  • Kodi zinthu zidzakhala bwanji dzikoli likadzatha?

Mungadabwe ndi mmene Baibulo likuyankhira mafunsowa m’magaziniyi ndipo mayankho ake akulimbikitsani kwambiri.

A Mboni za Yehova adzasangalala kukuthandizani kudziwa zambiri zokhudza cholinga cha Mulungu.