Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Kodi Anthu Amene Anamwalira Adzakhalanso Ndi Moyo?

Kodi Anthu Amene Anamwalira Adzakhalanso Ndi Moyo?

Imfa imakhudza aliyense. Koma kodi imfa ndi mathero a zonse? Kodi anthu amene anamwalira ndiye kuti basi anaiwalidwa? Kodi pali chiyembekezo chilichonse chokhudza anthu amene anamwalira?

TAONANI ZIMENE BAIBULO LIMANENA:

ANTHU AMENE ANAMWALIRA SANAIWALIDWE

“Onse ali m’manda achikumbutso . . . adzatuluka.”—Yohane 5:28, 29.

Mulungu sanaiwale anthu amene anamwalira ndipo adzaukitsa onse amene ali m’manda achikumbutso.

AKUFA ADZAUKITSIDWA PADZIKOLI

“Kudzakhala kuuka kwa olungama ndi osalungama omwe.”​—Machitidwe 24:15.

Anthu mamiliyoni ambirimbiri adzaukitsidwa n’kupatsidwa mwayi wokhala ndi moyo kwamuyaya m’dziko la mtendere.

CHIYEMBEKEZO CHOTI AKUFA ADZAUKITSIDWA N’CHODALIRIKA

“[Mulungu] amawerenga nyenyezi zonse, ndipo zonsezo amazitchula mayina ake.”​—Salimo 147:4.

Ngati Mulungu amakwanitsa kutchula nyenyezi iliyonse dzina, ndiye kuti akukumbukira anthu amene akufuna kudzawaukitsa.