Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Zochitika

Zochitika

Kuchitira Chifundo Anthu Onse

Tsiku lina mlongo wina wa ku New Zealand anaonera vidiyo pa jw.org yomwe inkafotokoza kuti Yehova samangomva chifundo mumtima koma amachisonyezanso. (Yes. 63:​7-9) Iye anaganiza zotsatira mfundo za muvidiyoyi pofufuza mpata woti athandize ena.Tsiku lomwelo atapita kukagula zinthu anakumana ndi mayi amene analibe pokhala ndipo anamufunsa ngati angafune kuti amugulire chakudya. Mayiyo anavomera. Mlongoyo atabwera ndi chakudya, anamulalikira mwachidule pogwiritsa ntchito kapepala kakuti, Kodi Mavuto Amene Tikukumana Nawowa Adzathadi?

Mayiyo anangoyamba kulira. Anafotokoza kuti anakulira m’banja la Mboni koma anasiya choonadi zaka zambiri m’mbuyomo. Koma chaposachedwa wakhala akupemphera kwa Yehova kuti amuthandize kubwerera kwa iye. Mlongoyo anamupatsa mayiyo Baibulo n’kukonza zoti aziphunzira naye. a

Mofanana ndi Yehova nafenso tikhoza kuchitira chifundo anthu kuphatikizapo achibale athu komanso abale ndi alongo mumpingo. Tingasonyezenso chifundo pofufuza mipata yoti tilalikire anthu ena.

a Kuti muone mmene mungathandizire anthu amene anafooka, onani nkhani yakuti “Bwererani kwa Ine” mu Nsanja ya Olonda ya June 2020.