Nkhani Zimene Zatuluka Pa Jw.Org
Kuyambira ndi magaziniyi, Nsanja ya Olonda izisonyeza nkhani zatsopano za m’gulu la nkhani zimene zinkatuluka m’magazini athu koma panopa zikutuluka pawebusaiti ya jw.org basi.
MFUNDO ZOTHANDIZA MABANJA
Mungatani Kuti Musamakwiye Mopitirira Malire?
Kupsa mtima kapena kusunga mkwiyo kukhoza kutidwalitsa. Ndiye kodi tingatani kuti tisamakwiye pakachitika zinthu zopsetsa mtima?
(Pitani pamene alemba kuti ZIMENE BAIBULO LIMAPHUNZITSA > ANTHU OKWATIRANA KOMANSO MABANJA.)
BAIBULO LIMASINTHA ANTHU
Misewu Ndi Imene Inali Nyumba Yanga
Antonio ankagwiritsa ntchito mankhwala osokoneza bongo, anali wachiwawa komanso ankaledzera ndipo ankadziona ngati wachabechabe. Kodi n’chiyani chinamuthandiza kuti asinthe?
(Pitani pamene alemba kuti ZIMENE BAIBULO LIMAPHUNZITSA > MTENDERE KOMANSO MOYO WOSANGALALA.)