Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Mungaphunzirenso Izi

Mungaphunzirenso Izi

Kodi mumakonda kuwerenga mbiri ya moyo wa abale ndi alongo athu?

Banja lina lomwe limawerenga nkhani imodzi m’mawa uliwonse linati: “Nkhanizi zimatilimbikitsa komanso kutithandiza kukhala osangalala. Zimatikumbutsa kuti nafenso tingakhale okhulupirika pa chilichonse.” Mlongo winanso yemwe amamva choncho analemba kuti: “Nkhanizi ndi zotonthoza, zolimbikitsa komanso zokhazika mtima pansi. Mbiri ya abale ndi alongo omwe amafotokozedwa imasonyeza kuti moyo wawo ndi watanthauzo. Zimandilimbikitsa kuti ndizichita zambiri mu utumiki komanso kuthandiza ana anga kuti adzachite utumiki wa nthawi zonse.”

Nkhanizi zingakuthandizeni kuti muzichita zambiri potumikira Yehova, musiye makhalidwe oipa komanso muzipirira mosangalala ndiponso mokhulupirika mayesero ovuta. Kodi mungapeze bwanji nkhanizi?

  • Fufuzani pa gawo lakuti “Mbiri za a Mboni za Yehova Ena” pa jw.org kapena pa JW Library®.

  • Fufuzani “Mbiri za a Mboni za Yehova Ena” pa Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI kapena Watchtower Library.