Mungaphunzirenso Izi
Mmene Mungagwiritsire Ntchito Gawo Lakuti “Zatsopano”
Pagawo lakuti “Zatsopano” pa JW Library komanso pa jw.org pamapezeka zinthu zomwe zangotulutsidwa kumene. Kodi mungagwiritse ntchito bwanji gawoli kuti mudziwe nkhani zimene zangochitika kumene?
JW Library
Nkhani iliyonse ikatulutsidwa, imaikidwa pagulu la nkhani zofanana ndi imene yangotuluka kumeneyo. Gulu la nkhanizo likaonekera pagawo lakuti “Zatsopano,” mukhoza kulipanga dawunilodi. Kenako mungawerenge nkhani yatsopano, yomwe imakhala pamwamba pa nkhani zonse. Nkhanizo zimasanjidwa potengera tsiku lomwe zinatuluka.
Mwina simungathe kuwerenga zinthu monga magazini pa nthawi imodzi. Pofuna kukuthandizani kudziwa magazini yomwe simunamalize kuwerenga, mungathe kuika magaziniyo pagawo lakuti Favorites, mpaka pamene mudzamalize kuiwerenga.
JW.ORG
Zinthu zina monga nkhani komanso zilengezo zimapezeka pa jw.org pokha osati pa JW Library. Muziona pafupipafupi gawo lakuti “Zatsopano” pawebusaitiyi kuti muone nkhani zatsopano.