Mawu Oyamba
Kodi mumasankha bwanji pakati pa zoyenera ndi zosayenera? Anthu ambiri amasankha zinthu potengera zimene chikumbumtima chawo chikuwauza kapenanso zimene anaphunzira kwa anthu ena. Pomwe ena amasankha zinthu potengera maganizo a anthu ena. Nanga inuyo n’chiyani chimakuthandizani kusankha pakati pa zoyenera ndi zosayenera? Kodi n’chiyani chingakuthandizeni kutsimikizira kuti zimene mungasankhe panopa zidzathandiza kwambiri inuyo komanso anthu a m’banja lanu?