Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

“Choonadi N’chiyani?”

“Choonadi N’chiyani?”

“Choonadi N’chiyani?”

KAZEMBE wachiroma Pontiyo Pilato ndiye anafunsa Yesu funsoli monyoza. Iye sankafuna yankho ndipo Yesu sanamuyankhe. Mwinamwake, Pilato ankaona kuti n’zosatheka kudziwa choonadi.​—Yohane 18:38.

Anthu ambiri masiku ano monga atsogoleri achipembedzo, aphunzitsi ndiponso andale ali ndi maganizo ngati a Pilato pankhani ya choonadi. Amakhulupirira kuti choonadi, makamaka pankhani ya makhalidwe ndi zinthu zauzimu, chimasinthasintha. Ngati zili choncho, ndiye kuti munthu aliyense angamasankhe yekha chabwino ndi choipa. (Yesaya 5:20, 21) Ndiponso, anthu angasiye kutsatira mfundo za makhalidwe abwino zimene makolo awo kale ankatsatira poganiza kuti tsabola wakale sawawa.

Tiyeni tione mawu amene anachititsa Pilato kufunsa funso limeneli. Yesu anali atanena kuti: “Chimene ndinabadwira, ndi chimene ndinabwerera m’dziko, ndicho kudzachitira umboni choonadi.” (Yohane 18:37) Yesu sankaona kuti n’zovuta kudziwa choonadi. Iye analonjeza ophunzira ake kuti: “Mudzadziwa choonadi, ndipo choonadi chidzakumasulani.”​—Yohane 8:32.

Kodi choonadi tingachipeze kuti? Panthawi ina, Yesu popemphera kwa Mulungu anati: “Mawu anu ndiwo choonadi” (Yohane 17:17) Baibulo ndi Mawu a Mulungu ndipo lili ndi choonadi chomwe chimapereka malangizo odalirika ndiponso chiyembekezo cha moyo wosatha.​—2 Timoteyo 3:15-17.

Pilato analibe chidwi chophunzira za choonadi. Nanga bwanji inuyo? Bwanji osafunsa Mboni za Yehova kuti mudziwe “choonadi” chimene Yesu ankaphunzitsa? Iwo angasangalale kukuuzani za choonadi chimenechi.