Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Tsiku Lofunika Kwambiri M’mbiri Yonse ya Anthu

Tsiku Lofunika Kwambiri M’mbiri Yonse ya Anthu

Tsiku Lofunika Kwambiri M’mbiri Yonse ya Anthu

Tsiku limeneli ndi tsiku limene Yesu Khristu anamwalira. N’chifukwa chiyani imfa ya Yesu inali yofunika kwambiri? Pali zifukwa zingapo.

Kukhulupirika kwa Yesu mpaka kufa kunasonyeza kuti munthu angathe kukhalabe wokhulupirika kwa Mulungu.

Imfa ya Khristu inapatsanso anthu ena mwayi wokalamulira naye kumwamba. Kuwonjezera apo, inatsegula njira yoti anthu ena ambiri adzasangalale ndi moyo wosatha m’paradaiso pa dziko lapansi.

Usiku woti mawa lake amwalira, Yesu anagwiritsa ntchito mkate wopanda chotupitsa ndi vinyo wofiira monga zizindikiro za nsembe ya thupi lake yomwe anaipereka mwachikondi. Ndipo anauza ophunzira ake kuti: “Muzichita zimenezi pondikumbukira ine.” (Luka 22:19) Kodi inuyo mudzakumbukira nawo mwambo wofunika kwambiri umenewu?

Mboni za Yehova zikukuitanani kuti mukakhale nazo limodzi pa Chikumbutso cha imfa ya Yesu. Chaka chino tsiku la Chikumbutso chimenechi ndi Lachinayi, April 9, dzuwa litalowa. Mukhoza kudzapita ku Nyumba ya Ufumu yomwe muli nayo pafupi. Funsani a Mboni za Yehova kwanuko kuti mudziwe nthawi ndi malo ake enieni.