NYIMBO 146
“Zinthu Zonse Zimene Ndikupanga Ndi Zatsopano”
-
1. Zizindikiro zikusonyezadi
Kuti Yesu akulamulira.
Anachotsa Satana kumwamba,
Posachedwa am’chotsa padziko.
(KOLASI)
Sangalalani chifukwa
Mulungu alidi nafe.
Iye adzachotsatu imfayi,
Chisoni ndiponso zopweteka.
Zonse zidzakhala zatsopano.
Mawuwa ndi oona.
-
2. Ona Yerusalemu watsopano.
Mkwatibwi wa Mwanawankhosayo
Atavala mochititsa chidwi.
Yehova ndiye kuwala kwake.
(KOLASI)
Sangalalani chifukwa
Mulungu alidi nafe.
Iye adzachotsatu imfayi,
Chisoni ndiponso zopweteka.
Zonse zidzakhala zatsopano.
Mawuwa ndi oona.
-
3. Mzindawu udzasangalatsa anthu.
Uzidzakhala wosatsekedwa.
Anthu azidzayenda mowala.
Atumikinu muziwalabe.
(KOLASI)
Sangalalani chifukwa
Mulungu alidi nafe.
Iye adzachotsatu imfayi,
Chisoni ndiponso zopweteka.
Zonse zidzakhala zatsopano.
Mawuwa ndi oona.
(Onaninso Mat. 16:3; Chiv. 12:7-9; 21:23-25.)