NYIMBO 158
“Sadzachedwa”
1. Dziko lopanda
nkhawa zonsezi
Ndi lomwe tonse
tikulakalaka.
Padziko lonse
zinthu zaipa
Tikudziwatu
muthetsa zonsezi.
(KOLASI)
Molezadi mtima
tikudikirira
Dzikotu latsopano.
Mapeto afika
posachedwa pompa.
Mawu anu akuti,
‘sadzachedwadi.’
2. Mulungu wathu
mudzaitana
Omwe anafa, ndipo
adzadzuka.
Zidzakhalatu
zosangalatsa!
Tithandizeni
kulezabe mtima.
(KOLASI)
Molezadi mtima
tikudikirira
Dzikotu latsopano.
Mapeto afika
posachedwa pompa.
Mawu anu akuti,
‘sadzachedwadi.’
3. Mumafufuza
mitima yathu
N’kutitonthoza ndi
chiyembekezo.
Tichite khama
polalikira.
Tikhale maso
nthawi yafupika.
(KOLASI)
Molezadi mtima
tikudikirira
Dzikotu latsopano.
Mapeto afika
posachedwa pompa.
Mawu anu akuti,
‘sadzachedwadi.’
Tiyembekezerebe.
(Onaninso Akol. 1:11.)