TIMABUKU TOTHANDIZA ANTHU KUTIDZIWA BWINO PADZIKO LONSE
A Mboni za Yehova Komanso Ntchito Zimene Angagwire M’malo mwa Usilikali
Kuyambira kale, malamulo akhala akunena kuti ndi ufulu wa munthu kusankha kugwira ntchito zina m’malo mwa usilikali. A Mboni amayamikira kwambiri maboma akamatsatira malamulowa n’kumawalola kugwira ntchito zosakhudzana ndi usilikali zomwe zingatukule madera amene amakhala.