Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

4 JANUARY, 2022
BRAZIL

Mvula Yamkuntho Yachititsa Madzi Kusefukira Kumpoto Chakum’mawa kwa Dziko la Brazil

Mvula Yamkuntho Yachititsa Madzi Kusefukira Kumpoto Chakum’mawa kwa Dziko la Brazil

Kuyambira pa 24 mpaka 26 December 2021, mvula yamphamvu inagwa ku Bahia State, m’dziko la Brazil ndipo anthu oposa 640,000 anakhudzidwa ndi mvulayi. Madzi osefukirawa anagumula madamu ndipo izi zinachititsa kuti mizinda yambiri isefukire komanso kuti anthu azunguliridwe ndi madzi n’kusowa kolowera.

Mmene Zinakhudzira Abale ndi Alongo Athu

  • Palibe aliyense amene anavulala

  • Ofalitsa 273 anakakamizika kusamuka m’nyumba zawo

  • Nyumba zokwana 109, zinawonongeka pang’ono

  • Nyumba za Ufumu zitatu zinawonongeka pang’ono

Ntchito Yopereka Chithandizo

  • Panakonzedwa Komiti Yothandiza Pangozi Zamwadzidzidzi kuti ipereke madzi, chakudya ndi zovala kwa anthu okhudzidwa

  • Ofalitsa omwe anasamuka m’nyumba zawo, akusungidwa ndi achibale awo komanso ofalitsa ena mongoyembekezera

  • Ntchito yopereka chithandizoyi ikugwiridwa motsatira njira zonse zodzitetezera ku COVID-19

M’bale Marcelo Ambrósio amene ali m’Komiti Yothandiza Pangozi Zamwadzidzidzi ananena kuti: “Kuona chikondi chimene abale ndi alongo anasonyezana pa nthawi yangoziyi, kwatilimbikitsa kuti tizitumikirabe Yehova mwakhama.”

Tikudziwa kuti Yehova apitiriza kukhala “malo okwezeka ndiponso achitetezo” kwa abale athu omwe anakhudzidwa ndi mvula yamkunthoyi​—Salimo 9:9.