Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Abale ndi alongo padziko lonse anasonkhana kuti achite Mwambo wa Chikumbutso

21 APRIL, 2022
NKHANI ZA PADZIKO LONSE

Anthu Mamiliyoni Anachita Mwambo Wokumbukira Imfa ya Khristu

Anthu Mamiliyoni Anachita Mwambo Wokumbukira Imfa ya Khristu

Abale akupatsana moni, m’dziko la Chile

Pa 15 April 2022, a Mboni za Yehova padziko lonse limodzi ndi anthu omwe anawaitana, anachita mwambo wa Chakudya Chamadzulo cha Ambuye. Aka kanali koyamba kuchita mwambo wofunikawu pamasom’pamaso kuchokera mu 2019. Omwe sanakwanitse kupita kumalo omwe kunkachitikira mwambowu, analumikizidwa kudzera pa zipangizo zamakono.

A Mboni za Yehova amaona kuti mwambo wapachakawu Wokumbukira Imfa ya Khristu, ndi wofunika kwambiri. Chifukwa cha mliri kwa COVID-19, zaka ziwiri zapitazi, mwambowu unachitika kudzera pa vidiyokomfelensi. Anthu oposa 21 miliyoni anapezeka pa Chikumbutso mu 2021.

Kwa anthu ena ngati Markensia Remy wa ku Haiti, kanali koyamba kuti apezeke pamwambowu pamasom’pamaso. Tsopano Markensia watha chaka kuchokera pomwe anabatizidwa. Iye ananena kuti: “Ndasangalala kwambiri kuti ndapezeka nawo pa Chikumbutso cha pa Nyumba ya Ufumu ndipo sindikudziwa kuti ndingafotokoze bwanji mmene ndasangalalira. Ndikuona kuti ndili m’banja labwino kwambiri.”

Tikuthokoza kwambiri chifukwa chokhala ndi mwayi wochita Mwambo wa Chikumbutso chaka chino. Tikuthokozanso kwambiri Yehova Mulungu ndi Mwana wake Yesu Khristu, chifukwa chachikondi chachikulu kwambiri chomwe anatisonyeza.​—Yohane 3:16.

 

Argentina

Bolivia

Brazil

Cambodia

Central African Republic

Cook Islands (Rarotonga)

Ecuador

Indonesia

Israel

Japan

Kazakhstan

Kosovo

Mexico

Paraguay

Peru

Philippines

Poland

Romania

Spain

Taiwan

Ukraine

United States

Venezuela