Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

AUGUST 17, 2020
MEXICO

Mphepo Yamkuntho (Hurricane Hanna) Yasakaza ku Mexico

Mphepo Yamkuntho (Hurricane Hanna) Yasakaza ku Mexico

Malo

Chigawo cha Tamaulipas ndi Nuevo León ku Mexico

Ngozi yake

  • Pa 26 July 2020, mphepo yamkuntho (Hurricane Hanna) inawomba motsetsereka kumpoto chakum’mawa kwa Mexico ndipo inachititsa kuti madzi ambiri asefukire

Mmene mphepoyi yakhudzira abale ndi alongo athu

  • Ku Nuevo León, mabanja 14 anasamutsidwa m’nyumba zawo pofuna kupewa ngoziyi

  • Mumzinda wa Reynosa, ku Tamaulipas, ofalitsa 100 anasamuka m’nyumba zawo

Katundu amene wawonongeka

  • Nyumba 21 zawonongeka ku Nuevo León

  • Nyumba 117 zawonongeka ku Tamaulipas

Ntchito yothandiza anthu

  • Ofesi ya Nthambi ya Central America yakhazikitsa Makomiti Othandiza pa Ngozi Zogwa Mwadzidzidzi

  • Oyang’anira madera ndi akulu a mipingo m’madera okhudzidwawa, akuyendetsera limodzi ntchito yoyeretsa ndi kuthira mankhwala opha majeremusi m’nyumba zomwe munalowa madzi osefukira

  • Ambiri mwa abale ndi alongo omwe anasamutsidwa m’nyumba zawo ku Nuevo León, panopa abwereranso kwawo

  • Ku Tamaulipas, abale ndi alongo am’mipingo yosiyanasiyana akupereka chakudya ndi zovala kwa anthu amene anakhudzidwa ndi ngoziyi

Tikuthokoza Yehova chifukwa chakuti palibe m’bale kapena mlongo aliyense amene wavulala pangoziyi. Ntchito yothandiza abale athu yomwe yayamba kale kuchitikayi ikusonyeza kuti nthawi zonse Atate wathu wakumwamba ndi anthu ake amakhala “thandizo lopezeka mosavuta pa nthawi ya masautso.”​—Salimo 46:1.