Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

M’bale Sai Asher akukamba nkhani ya Chikumbutso

APRIL 21, 2021
MYANMAR

Mwambo Wokumbukira Imfa ya Khristu wa 2021​—Myanmar

Nkhani ya Chikumbutso Inakambidwa pa Nthawi ya Ziwawa Kudzera pa Telefoni

Mwambo Wokumbukira Imfa ya Khristu wa 2021​—Myanmar

Kuyambira mu February 2021, m’dziko la Myanmar mwakhala mukuchitika ziwawa. Kutatsala ma wiki ochepa kuti mwambo wokumbukira imfa ya Khristu uchitike, anthu anayamba kumenyana m’madera osiyanasiyana m’dzikoli. Zimenezi zinachititsa kuti ofalitsa ambiri pa ofalitsa 5,102 omwe ali m’dzikoli azilephera kugwiritsa ntchito Intaneti. Choncho abale anamvetsera nkhani ya Chikumbutso kudzera pa telefoni.

Mu mzinda wina, pa tsiku la Chikumbutso, anthu anayamba kuwomberana kwambiri m’misewu. Asilikali anayamba kuyenda nyumba iliyonse kufufuza anthu amene ankachita ziwonetsero. Pa nthawiyi, abale analimbikitsidwa ndi mawu a mu lemba lachaka chino la Yesaya 30:15 kuti ayenera ‘kukhala osatekeseka ndi kukhulupirira Yehova.’ Abalewa anabisala m’nyumba zawo ndipo anaonetsetsa kuti asamalankhule mokweza komanso kuti m’nyumbamo musamawale kwambiri moti anachita mwambo wa Chikumbutso popanda mavuto ena alionse. Ngakhale kunali ziwawa, pa mwambowu panapezeka anthu ambiri kuposa m’mbuyo monsemu. Ambiri anamvetsera nkhaniyi kudzera pa telefoni.

Anthu amene anapezeka pa mwambo wa Chikumbutso m’dzikoli, analipo 11,877. Chiwerengerochi chinaposa cha mu 2019 ndi 14 peresenti.

Alongo awiri akugwiritsa ntchito tabuleti kumvetsera nkhani ya Chikumbutso pa intaneti. Analumikizanso sipika kuti ena azitha kumvetsera nawo kudzera pa foni

Tili ndi chikhulupiriro kuti Atate wathu wakumwamba, Yehova Mulungu, amasangalala akamaona abale akupitirizabe kumulambira molimba mtima ngakhale pa nthawi imene kukuchitika ziwawa.​—Miyambo 27:11.