Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Russia

 

2016-03-02

RUSSIA

Khoti la ku Taganrog Lagamula kuti a Mboni za Yehova 16 Ndi Olakwa Chifukwa Chochita Zachipembedzo

Chigamulochi chingachititse kuti a Mboni apitirize kuzunzidwa ndiponso kumangidwa chifukwa cha chipembedzo chawo ku Russia.

2016-03-04

RUSSIA

Zimene Mneneri wa Mboni za Yehova Ananena Zokhudza Mlandu wa ku Taganrog, M’dziko la Russia

Kuyambira mu 2011, a Mboni 16 akhala akuimbidwa mlandu chifukwa chochita zachipembedzo chawo. Kodi n’zoona kuti ali ndi mlandu wochita zinthu zoopsa zimene zingabweretse chisokonezo?

2016-02-17

RUSSIA

Akatswiri Ena Sanagwirizane ndi Zimene Dziko la Russia Lachita Poletsa JW.ORG

Pa 21 July 2015 dziko la Russia linaletsa webusaiti yovomerezeka ya Mboni za Yehova ya jw.org ndipo dzikoli ndi loyamba kuchita zimenezi.

2016-02-18

RUSSIA

Wa Mboni Wina wa ku Russia Anatola Ndalama Zokwana Mayuro 6,000 Ndipo Anazibweza kwa Mwini Wake

Mayi Svetlana Nemchinova, omwe ndi a Mboni za Yehova, anafufuza mwini wa ndalama zomwe zinatayidwa mwangozi pamalo ena.

2015-03-17

RUSSIA

Kodi Khoti la Rostov Ligamula Zotani pa Mlandu Umene a Mboni za Yehova Apanga Apilo?

Pa December 11, 2014, khoti la m’chigawo cha Rostov lidzamvetsera mlandu wa apilo wa a Mboni za Yehova 16 a ku Taganrog, m’dziko la Russia. Iwo akuimbidwa mlandu womwe akuti anachita zinthu zosokoneza maganizo a anthu.

2014-12-03

RUSSIA

Khoti Lalikulu Kwambiri ku Russia Lipitiriza Kuzenga Mlandu Wokhudza Kutsekedwa kwa Bungwe la Mboni la ku Samara

Pa November 12, 2014, Khoti Lalikulu Kwambiri ku Russia lakonza zoti lipitirize kuzenga mlandu wa apilo wokhudza kutsekedwa kwa bungwe lovomerezeka ndi boma la Russia la Mboni za Yehova la ku Samara.

2014-10-22

RUSSIA

A Mboni za Yehova a ku Samara Apanga Apilo Mlandu Wokhudza Kutsekedwa kwa Bungwe Lawo Lovomerezeka ndi Boma Kukhoti Lalikulu Kwambiri la ku Russia

Khoti Lalikulu Kwambiri la ku Russia liweruza mlandu umene a Mboni za Yehova a ku Samara apanga apilo. Mlanduwu ndi wokhudza kutsekedwa kwa bungwe lawo lovomerezeka ndi boma komanso woti bungweli limachita zinthu monyanyira komanso zosokoneza maganizo a anthu.

2014-08-19

RUSSIA

Khoti la ku Taganrog Lapeza a Mboni za Yehova Kuti ndi Olakwa Chifukwa Chochita Zinthu Zokhudzana ndi Chipembedzo Chawo

Ufulu wolambira wa a Mboni 160,000 ku Russia, uli pangozi chifukwa cha chigamulochi.

2014-07-29

RUSSIA

A Mboni za Yehova Akuimbidwa Mlandu ku Taganrog

Anthu akuphwanyiridwa ufulu wachipembedzo ku Russia. Mvetserani zimene ena mwa a Mboni 16 komanso maloya awo ananena.

2014-07-29

RUSSIA

Khoti Loona za Ufulu wa Anthu ku Ulaya Ladzudzulanso Boma la Russia Chifukwa Chophwanyira Anthu Ufulu Wachipembedzo

Chigamulo chachitatuchi chikusonyeza kuti Khoti Loona za Ufulu wa Anthu ku Ulaya likuona kuti dziko la Russia likuphwanya ufulu wachibadwidwe wa a Mboni za Yehova, monga ufulu wolambira mwamtendere.

2014-06-17

RUSSIA

Mlandu Wokhudza Anthu Ena a Mboni za Yehova Mumzinda wa Taganrog ku Russia Ukupitirirabe

Anthu 16 akuimbidwa mlandu chifukwa cholambira Mulungu. Ngati angapezeke kuti ndi olakwa ndiye kuti ufulu umene anthu ali nawo wolambira Mulungu udzasokonezedwa m’dziko lonse la Russia.