Russia
Anthu Ena ku Russia Akuphwanyiridwa Ufulu Wawo Wolambira
A Mboni za Yehova akuimbidwa milandu m’tauni yaing’ono ya Taganrog. Akuluakulu a boma alanda mabuku ndiponso Nyumba ya Ufumu ya a Mboni za Yehova.
Anthu Ena a ku Russia Akuimbidwa Mlandu Chifukwa cha Chikhulupiriro Chawo
Ngati anthu a Mboni za Yehova omwe akuimbidwa milandu m’dera la Taganrog angapezeke kuti ndi olakwa, ndiye kuti zimenezi zidzasokoneza ufulu wachibadwidwe wa anthu ambiri m’dziko la Russia.
Khoti Lalikulu ku Russia Lakana Zoti Webusaiti ya JW.ORG Itsekedwe
Khoti lalikulu la Tver ku Russia lakana zimene khoti laling’ono linagamula zoti webusaiti yovomerezeka ya Mboni za Yehova, ya jw.org, itsekedwe.
Kupitiriza Nkhani: Mapulani Ofuna Kuletsa Webusaiti ya JW.ORG Alephereka
Khoti lalikulu linasintha chigamulo choti webusaiti ya jw.org iletsedwe m’dziko la Russia.
Akuluakulu a Boma la Russia Akufuna Kuletsa Webusaiti ya JW.ORG
Khoti la Tsentralniy District lomwe lili mumzinda wa Tver linagamula kuti webusaiti ya jw.org iletsedwe m’dziko la Russia. Koma a Mboni za Yehova achita apilo.
Khoti la ku Ulaya Lateteza Ufulu wa Mboni za Yehova pa Mlandu Wokhudza Kusungiridwa Chinsinsi
Khoti Loona za Ufulu wa Anthu ku Ulaya lalamula boma la Russia kuti lipereke chipukuta misozi kwa anthu amene linawaphwanyira ufulu wachibadwidwe wofunika kwambiri wokhudza kusungiridwa chinsinsi.
Khoti Linagamula kuti, “Sitili M’chaka cha 1937”
Woweruza milandu wa m’bwalo la milandu lalikulu ku Russia anatsutsa chigamulo chimene khoti laling’ono linalamula
Mavuto Amene a Mboni Akhala Akukumana Nawo kwa Zaka 10 pa Nkhani Zamalamulo Anaunikidwa pa Tsiku la 5 Lozenga Mlandu ku Khoti Lalikulu Kwambiri ku Russia
Maloya oimira Unduna wa Zachilungamo sanathe kunena chifukwa chomveka chokhudza malamulo chochititsa kuti Likulu la Mboni za Yehova litsekedwe ku Russia.
Akatswiri Ena Akana Kuti Boma la Russia Liletse Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Nkhaniyi ndi yachiwiri pa nkhani zitatu zomwe zikufotokoza zimene ananena akatswiri a zachipembedzo, a zandale, zachikhalidwe cha anthu komanso a maphunziro a ulamuliro wa Soviet Union.
Khoti Lalikulu Kwambiri M’dziko la Russia Silinasinthe Chigamulo Chimene Linapereka Choletsa Ntchito ya Mboni za Yehova
Khoti Lalikulu Kwambiri M’dziko la Russia silinasinthe chigamulo chimene linapereka pa 20 April, 2017. A Mboni za Yehova ku Russia apanga apilo za nkhaniyi ku Khoti Loona za Ufulu wa Anthu ku Ulaya komanso ku Komiti ya United Nations Yoona za Ufulu wa Anthu.
A Mboni za Yehova Akuvutika Kwambiri Chifukwa cha Chigamulo cha Khoti Lalikulu Kwambiri ku Russia
Chigamulo cha khoti chachititsa kuti anthu ambiri azidana ndi a Mboni ndipo chapereka mphamvu kwa anthu komanso akuluakulu a boma kuti aziwachitira nkhanza.