20 JANUARY, 2022
RUSSIA
Abale 7 a Ku Russia Akupitiriza Kupeza Mphamvu Chifukwa Chodalira Yehova
Khoti la mumzinda wa Pechora ku Komi, posachedwa lipereka chigamulo chake pa mlandu wa M’bale Nikolay Anufriyev, Eduard Merinkov, Gennadiy Polyakevich, Aleksandr Prilepskiy, Viktor Shchannikov, Gennadiy Skutelets ndi Aleksandr Vorontsov. Loya woimira boma sananenebe chilango chimene akufuna kuti abalewa apatsidwe.
Nthawi Komanso Zimene Zinachitika
28 January, 2020
Apolisi anakafufuza zinthu m’nyumba 12 za a Mboni za Yehova ku Komi. M’bale Polyakevich ndi M’bale Skutelets, anawatsegulira mlandu
30 January, 2020
M’bale Gennadiy Polyakevich anatsekeredwa m’ndende poyembekezera kuzengedwa mlandu. Ndipo M’bale Gennadiy Skutelets anagamulidwa kuti akhale pa ukaidi wosachoka pakhomo
20-25 May, 2020
Apolisi anapanikiza ndi mafunso abale ndi alongo ena a ku Pechora ndi cholinga chofuna kupeza anthu omwe angawagwiritse ntchito ngati mboni pa mlanduwu. Chifukwa choopsezedwa ndi apolisi ochita kafukufuku, m’bale wina anachita sitiroko koma panopo ali bwino
26 June , 2020
M’bale Gennadiy Polyakevich anamuwonjezera masiku omusunga poyembekezera kuzengedwa kwa mlandu wake. Jaji ananena kuti M’bale Polyakevich anamupeza ndi mlandu “wopalamula mlandu mwadala” komanso chifukwa chonena kuti “apitiriza kutumikira Yehova ngakhale kuti akuzunzidwa ndi akuluakulu a boma”
24 August, 2020
Apolisi anakafufuza zinthu m’nyumba zina 12 za abale ndi alongo
10 November, 2020
Apolisi anatsegulira mlandu M’bale Aleksandr Prilepskiy, Aleksandr Vorontsov, Eduard Merinkov, Nikolay Anufriyev ndi Viktor Shchannikov. Ndipo mlanduwu anauphatikiza ndi mlandu wa M’bale Gennadiy Polyakevich ndi Gennadiy Skutelets
25 November, 2020
M’bale Gennadiy Polyakevich atasungidwa kwa masiku 300 poyembekezera mlandu wake, anamasulidwa n’kuikidwa pa ukaidi wosachoka pakhomo
27 January, 2021
M’bale Gennadiy Skutelets anamasulidwa, atakhala pa ukaidi wosachoka pakhomo kwa masiku 363
Zokhudza Abalewa
Tili ndi chikhulupiriro kuti abale athu adzapeza madalitso panopo komanso m’tsogolo chifukwa chokhulupirira ubwino wa Yehova.—Salimo 27:13.