JULY 14, 2021
RUSSIA
Kukonzekereratu Chizunzo Kunathandiza Abale Atatu Kukhalabe Okhulupirika kwa Yehova
Nthawi Komanso Zimene Zinachitika
Khoti la m’Boma la Ussuriyskiy m’Chigawo cha Primorye posachedwapa lilengeza chigamulo chake pa mlandu wa abale awa: Anton Chermnykh, Sergey Korolchuk ndi Dmitriy Tishchenko. * Loya woimira boma pa mlandu akuyembekezeka kupempha kuti abalewa akakhale kundende
23 September 2020
A khoti anayamba kumvetsera mlandu wa Anton, Sergey ndi Dmitriy
7 July 2020
Abalewa, Anton, Sergey ndi Dmitriy akuwazenga mlandu woti ndi atsogoleri a gulu la chipembedzo lomwe ndi loletsedwa chifukwa limachita zinthu zoopsa
18 June 2019
M’bale Sergey anamutsekera m’ndende masiku awiri poyembekezera kumuzenga mlandu
Zokhudza Abalewa
Pamene mlandu wawo ukupitirira, tikudziwa kuti Yehova adalitsa kukhulupirika kwa Anton, Sergey, ndi Dmitriy.—Miyambo 28:20.
^ N’zovuta kudziwiratu tsiku lenileni limene khoti lidzapereke chigamulo