23 MARCH, 2022
RUSSIA
Yehova Anathandiza Abale ndi Alongo Okhulupirika Okwana 6
Posachedwa khoti la m’Boma la Industrialniy m’Chigawo cha Khabarovsk, lipereka chigamulo pa mlandu wa Mlongo Maya Karpushkina, M’bale Stanislav Kim, M’bale Nikolay Polevodov, Mlongo Svetlana Sedova, M’bale Vitaliy Zhuk ndi mkazi wake Tatyana. Loya waboma sananene kuti anthuwa apatsidwe chilango chotani.
Nthawi Komanso Zimene Zinachitika
10 November, 2018
Apolisi anasokoneza pate yomwe anthu 55 ankachita. Onse omwe ankachita pateyo kuphatikizapo ana, anapanikizidwa ndi mafunso, kutenga zidindo za zala zawo komanso kuwajambula zithunzi
12 November, 2018
M’bale Kim, M’bale Polevodoc ndi M’bale Zhuk anakawatsekera m’ndende poyembekezera kuwazenga mlandu. Mlongo Karpushkina ndi Mlongo Zhuk anawaletsa kuti asatuluke m’dera lomwe amakhala
14 January, 2019
M’bale Polevodoc ndi M’bale Zhuk anawatulutsa m’ndende n’kuwaika pa ukaidi wosachoka pakhomo
29 January, 2019
M’bale Kim anamutulutsa m’ndende n’kumuika pa ukaidi wosachoka pakhomo
18 July, 2019
Mlandu anausamutsira ku khoti la m’Boma la Industrialniy m’Chigawo cha Khabarovsk
2 August, 2019
M’bale Polevodoc anamasulidwa pa ukaidi wosachoka pakhomo
9 September, 2019
Mlandu wina wokhudza M’bale Kim komanso M’bale Polevodoc, unakaperekedwa kukhoti la Khabarovsk m’Boma la Zheleznodorozhniy
5 November, 2019
M’bale Polevodoc anamuletsa kutuluka m’dera lomwe ankakhala
18 January, 2020
M’bale Kim ndi M’bale Zhuk, anawamasula pa ukaidi wosachoka pakhomo
4 February, 2020
M’bale Kim ndi M’bale Polevodoc anawapeza kuti ndi olakwa pa mlandu wina ndipo aliyense anagamulidwa kuti kwa zaka ziwiri, azitsatira malamulo ena ali kunyumba kwawo. Pa nthawi yonseyi Khoti la Khabarovsk la m’Boma la Zheleznodorozhniy, liziwayang’anira monga anthu opalamula mlandu
3 August, 2020
Mlandu womwe unali ku Khoti la m’Boma la Industrialniy anaubweza kwa loya woimira boma ndipo loyayu anachita apilo
29 September, 2020
Khoti la m’Chigawo cha Khabarovsk linalandira apilo ya loya waboma. M’bale Kim ndi M’bale Polevodoc anakaonekera pamaso pa jaji. Jajiyo anafotokoza kuti Dziko la Russia, mogwirizana ndi mayiko ena onse, linasainira nawo mgwirizano wa mayiko womwe umaletsa kuphwanya ufulu wopembedza kwa nzika zake
12 October, 2020
Khoti la m’Chigawo cha Khabarovsk linagwirizana ndi chigamulo chomwe khoti la m’Boma la Industrialniy linapereka ndipo linabweza mlandu kwa loya waboma
15 December, 2021
Mlandu unabwereranso ku khoti la m’Boma la Industrialniy
Zokhudza abale ndi alongowa
Tikudziwa kuti Yehova apitiriza kuthandiza abale ndi alongo athuwa komanso ena ambiri omwe akupanga “mtambo wa mboni waukulu” wamasiku athu ano.—Aheberi 12:1.