1 JANUARY 2024
RUSSIA
‘Yehova Sanandisiyepo’
Posachedwapa khoti la mumzinda wa Kurgan m’chigawo cha Kurgan, lipereka chigamulo chake pa mlandu wokhudza M’bale Anatoliy Isakov. Loya woimira boma pa mlanduwu, adzafotokozabe chilango chomwe akufuna kuti m’baleyu apatsidwe.
Zokhudza M’baleyu
Timayamikira a Isakov chifukwa chokhala chitsanzo chabwino pa nkhani yolimba mtima komanso posonyeza chikhulupiriro ngakhale kuti akukumana ndi mavuto ambiri. Ndipo ndife oyamikira kwambiri kudziwa kuti kaya tikumane ndi zotani pa moyo wathu, Yehova adzapitiriza kukhala ‘thanthwe la mitima yathu.’—Salimo 73:26.
Nthawi ndi Zochitika
13 July 2021
Anawatsegulira mlandu
14 July 2021
Apolisi anakafufuza m’nyumba yawo. Anaikidwa m’ndende kwa kanthawi kochepa
15 July 2021
Anawasamutsira kundende poyembekezera kuwazenga mlandu
21 July 2021
Anachita apilo kudipatimenti yoona za umoyo ya m’chigawo cha Kurgan kuti awamasule n’cholinga choti azikalandira thandizo la matenda a khansa
28 August 2021
Anatulutsidwa m’ndende poyembekezera kuzenga mlandu wawo, Khoti Loona za Ufulu wa Anthu ku Europe litalamula koma analetsedwa kupita m’madera ena
6 July 2023
Mlandu unayamba kuzengedwa