Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

SEPTEMBER 17, 2020
UNITED STATES

Moto Ukupitirira Kuwononga Zinthu Kumadzulo kwa United States

Moto Ukupitirira Kuwononga Zinthu Kumadzulo kwa United States

Malo

California, Oregon ndi Washington

Ngozi yake

  • Moto wolusa womwe ukufalikira mofulumira kwambiri wawononga malo okwana mahekitala oposa 2 miliyoni kuchokera ku California mpaka ku Washington

  • Motowu wachititsa kuti anthu azipuma mpweya wowonongeka

  • Moto umene wawononga ku California waposa moto wina wonse womwe wakhala ukuyaka kumeneko m’mbuyo monsemu

Mmene motowu wakhudzira abale ndi alongo athu

  • Ofalitsa 4,546 asamuka m’nyumba zawo

Katundu amene wawonongeka

  • Nyumba 61 zapseratu

  • Nyumba 16 zawonongeka

Ntchito yothandiza anthu

  • Makomiti Othandiza pa Ngozi Zogwa Mwadzidzidzi akupitirizabe kugwira ntchito limodzi ndi oyang’anira madera komanso akulu a m’mipingo pothandiza abale ndi alongo amene asamuka m’nyumba zawo, kwinaku akutsatira malangizo opewera matenda a COVID-19

Ofalitsa omwe akhudzidwa ndi motowu akuyamikira kwambiri zimene Yehova wachita powathandiza kudzera m’gulu lake. Mlongo wina amene nyumba yake inapsa ananena kuti abale anali “ofunitsitsa kutichitira china chilichonse chimene tinkafunikira, ifeyo tisanadziwe n’komwe kuti tikufunikira zimenezo.”

Ngakhale kuti abale ndi alongo amene akhudzidwa ndi motowu akuvutikabe, iwo akuona kuti Yehova akupitiriza kuwasamalira mwachifundo.—Yakobo 5:11.