Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

7 SEPTEMBER, 2020
UNITED STATES

Mphepo Yamkuntho Yotchedwa Hurricane Laura Yawononga ku Louisiana

Mphepo Yamkuntho Yotchedwa Hurricane Laura Yawononga ku Louisiana

Malo

Arkansas, Mississippi, kumadzulo kwa Louisiana ndi kum’mawa kwa Texas

Ngozi yake

  • Chimphepo champhamvu chinasakaza zinthu kumadzulo kwa Louisiana pa 27 August 2020 ndipo magetsi anazima

Mmene yakhudzira abale ndi alongo

  • N’zomvetsa chisoni kuti mlongo wina wachikulire anamwalira pamene ankasamutsidwa kumalo amene ankalandira chithandizo chakuchipatala

  • Mlongo wina anavulala pang’ono

  • Ofalitsa 3,992 anasamutsidwa kunyumba zawo

Zinthu zimene zawonongeka

  • Nyumba 10 za abale zawonongekeratu

  • Nyumba 95 ndi Nyumba za Ufumu 4 zawonongeka kwambiri

  • Nyumba 192 ndi Nyumba za Ufumu 16 zawonongeka pang’ono

Kuthandiza amene akhudzidwa

  • Nthambi ya ku United States yakhazikitsa komiti yoti ithandize pa ngozi imeneyi

  • Oyang’anira madera ndi akulu m’mipingo akuthandiza ofalitsa amene asamutsidwa kuti apeze malo okhala

Zimene zachitika

  • Abale a m’madera apafupi analola kuti akhristu anzawo adzafikire m’nyumba zawo koma ankayesetsa kuchita zonse zothandiza popewa COVID-19. M’bale wina amene anasamutsidwa anati: “Zonsezi ndi umboni wakuti Yehova akutidalitsa!”

Abale ndi alongo amene ayesetsa kutsatira malangizo komanso kuthandiza anzawo amene akhudzidwa ‘asonyeza kuti iwowo ndi atumiki a Mulungu’ enieni.—2 Akorinto 6:4.